< Proverbs 26 >

1 As snow in summer, and as rain in harvest, so honour is not seemly for a fool.
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 As the wandering sparrow, as the flying swallow, so the curse that is causeless shall come home.
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 A whip for the horse, a bridle for the ass, and a rod for the back of fools.
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 Answer not a fool according to his folly, lest thou also be like unto him.
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 Answer a fool according to his folly, lest he be wise in his own eyes.
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 He that sendeth a message by the hand of a fool cutteth off his own feet, and drinketh damage.
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 The legs hang limp from the lame; so is a parable in the mouth of fools.
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 As a small stone in a heap of stones, so is he that giveth honour to a fool.
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 As a thorn that cometh into the hand of a drunkard, so is a parable in the mouth of fools.
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 A master performeth all things; but he that stoppeth a fool is as one that stoppeth a flood.
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 As a dog that returneth to his vomit, so is a fool that repeateth his folly.
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 Seest thou a man wise in his own eyes? there is more hope of a fool than of him.
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 The sluggard saith: 'There is a lion in the way; yea, a lion is in the streets.'
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 The door is turning upon its hinges, and the sluggard is still upon his bed.
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 The sluggard burieth his hand in the dish; it wearieth him to bring it back to his mouth.
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 The sluggard is wiser in his own eyes than seven men that give wise answer.
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 He that passeth by, and meddleth with strife not his own, is like one that taketh a dog by the ears.
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 As a madman who casteth firebrands, arrows, and death;
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 So is the man that deceiveth his neighbour, and saith: 'Am not I in sport?'
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 Where no wood is, the fire goeth out; and where there is no whisperer, contention ceaseth.
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 As coals are to burning coals, and wood to fire; so is a contentious man to kindle strife.
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 The words of a whisperer are as dainty morsels, and they go down into the innermost parts of the body.
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 Burning lips and a wicked heart are like an earthen vessel overlaid with silver dross.
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 He that hateth dissembleth with his lips, but he layeth up deceit within him.
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 When he speaketh fair, believe him not; for there are seven abominations in his heart.
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 Though his hatred be concealed with deceit, his wickedness shall be revealed before the congregation.
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 Whoso diggeth a pit shall fall therein; and he that rolleth a stone, it shall return upon him.
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 A lying tongue hateth those that are crushed by it; and a flattering mouth worketh ruin.
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

< Proverbs 26 >