< Proverbs 23 >
1 When thou sittest to eat with a ruler, consider well him that is before thee;
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 And put a knife to thy throat, if thou be a man given to appetite.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Be not desirous of his dainties; seeing they are deceitful food.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Weary not thyself to be rich; cease from thine own wisdom.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Wilt thou set thine eyes upon it? it is gone; for riches certainly make themselves wings, like an eagle that flieth toward heaven.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Eat thou not the bread of him that hath an evil eye, neither desire thou his dainties;
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 For as one that hath reckoned within himself, so is he: 'Eat and drink', saith he to thee; but his heart is not with thee.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 The morsel which thou hast eaten shalt thou vomit up, and lose thy sweet words.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Speak not in the ears of a fool; for he will despise the wisdom of thy words.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Remove not the ancient landmark; and enter not into the fields of the fatherless;
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 For their Redeemer is strong; He will plead their cause with thee.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Apply thy heart unto instruction, and thine ears to the words of knowledge.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Withhold not correction from the child; for though thou beat him with the rod, he will not die.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Thou beatest him with the rod, and wilt deliver his soul from the nether-world. (Sheol )
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol )
15 My son, if thy heart be wise, my heart will be glad, even mine;
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 Yea, my reins will rejoice, when thy lips speak right things.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Let not thy heart envy sinners, but be in the fear of the LORD all the day;
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 For surely there is a future; and thy hope shall not be cut off.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Hear thou, my son, and be wise, and guide thy heart in the way.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Be not among winebibbers; among gluttonous eaters of flesh;
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 For the drunkard and the glutton shall come to poverty; and drowsiness shall clothe a man with rags.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Hearken unto thy father that begot thee, and despise not thy mother when she is old.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Buy the truth, and sell it not; also wisdom, and instruction, and understanding.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 The father of the righteous will greatly rejoice; and he that begetteth a wise child will have joy of him.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Let thy father and thy mother be glad, and let her that bore thee rejoice.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 My son, give me thy heart, and let thine eyes observe my ways.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 For a harlot is a deep ditch; and an alien woman is a narrow pit.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 She also lieth in wait as a robber, and increaseth the faithless among men.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Who crieth: 'Woe'? who: 'Alas'? who hath contentions? who hath raving? who hath wounds without cause? who hath redness of eyes?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 They that tarry long at the wine; they that go to try mixed wine.
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Look not thou upon the wine when it is red, when it giveth its colour in the cup, when it glideth down smoothly;
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 At the last it biteth like a serpent, and stingeth like a basilisk.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Thine eyes shall behold strange things, and thy heart shall utter confused things.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 Yea, thou shalt be as he that lieth down in the midst of the sea, or as he that lieth upon the top of a mast.
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 'They have struck me, and I felt it not, they have beaten me, and I knew it not; when shall I awake? I will seek it yet again.'
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”