< Proverbs 18 >
1 He that separateth himself seeketh his own desire, and snarlest against all sound wisdom.
Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
2 A fool hath no delight in understanding, but only that his heart may lay itself bare.
Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
3 When the wicked cometh, there cometh also contempt, and with ignominy reproach.
Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
4 The words of a man's mouth are as deep waters; a flowing brook, a fountain of wisdom.
Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
5 It is not good to respect the person of the wicked, so as to turn aside the righteous in judgment.
Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
6 A fool's lips enter into contention, and his mouth calleth for strokes.
Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
7 A fool's mouth is his ruin, and his lips are the snare of his soul.
Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
8 The words of a whisperer are as dainty morsels, and they go down into the innermost parts of the belly.
Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
9 Even one that is slack in his work is brother to him that is a destroyer.
Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
10 The name of the LORD is a strong tower: the righteous runneth into it, and is set up on high.
Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
11 The rich man's wealth is his strong city, and as a high wall in his own conceit.
Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
12 Before destruction the heart of a man is haughty, and before honour goeth humility.
Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
13 He that giveth answer before he heareth, it is folly and confusion unto him.
Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
14 The spirit of a man will sustain his infirmity; but a broken spirit who can bear?
Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
15 The heart of the prudent getteth knowledge; and the ear of the wise seeketh knowledge.
Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
16 A man's gift maketh room for him, and bringeth him before great men.
Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
17 He that pleadeth his cause first seemeth just; but his neighbour cometh and searcheth him out.
Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
18 The lot causeth strife to cease, and parteth asunder the contentious.
Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
19 A brother offended is harder to be won than a strong city; and their contentions are like the bars of a castle.
Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
20 A man's belly shall be filled with the fruit of his mouth; with the increase of his lips shall he be satisfied.
Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
21 Death and life are in the power of the tongue; and they that indulge it shall eat the fruit thereof.
Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
22 Whoso findeth a wife findeth a great good, and obtaineth favour of the LORD.
Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
23 The poor useth entreaties; but the rich answereth impudently.
Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
24 There are friends that one hath to his own hurt; but there is a friend that sticketh closer than a brother.
Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.