< Proverbs 17 >

1 Better is a dry morsel and quietness therewith, than a house full of feasting with strife.
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
2 A servant that dealeth wisely shall have rule over a son that dealeth shamefully, and shall have part of the inheritance among the brethren.
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
3 The refining pot is for silver, and the furnace for gold; but the LORD trieth the hearts.
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
4 A evil-doer giveth heed to wicked lips; and a liar giveth ear to a mischievous tongue.
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
5 Whoso mocketh the poor blasphemeth his Maker; and he that is glad at calamity shall not be unpunished.
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
6 Children's children are the crown of old men; and the glory of children are their fathers.
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
7 Overbearing speech becometh not a churl; much less do lying lips a prince.
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
8 A gift is as a precious stone in the eyes of him that hath it; whithersoever he turneth, he prospereth.
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
9 He that covereth a transgression seeketh love; but he that harpeth on a matter estrangeth a familiar friend.
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
10 A rebuke entereth deeper into a man of understanding than a hundred stripes into a fool.
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
11 A rebellious man seeketh only evil; therefore a cruel messenger shall be sent against him.
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
12 Let a bear robbed of her whelps meet a man, rather than a fool in his folly.
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
13 Whoso rewardeth evil for good, evil shall not depart from his house.
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
14 The beginning of strife is as when one letteth out water; therefore leave off contention, before the quarrel break out.
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
15 He that justifieth the wicked, and he that condemneth the righteous, even they both are an abomination to the LORD.
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
16 Wherefore is there a price in the hand of a fool to buy wisdom, seeing he hath no understanding?
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
17 A friend loveth at all times, and a brother is born for adversity.
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
18 A man void of understanding is he that striketh hands, and becometh surety in the presence of his neighbour.
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
19 He loveth transgression that loveth strife; he that exalteth his gate seeketh destruction.
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
20 He that hath a froward heart findeth no good; and he that hath a perverse tongue falleth into evil.
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
21 He that begetteth a fool doeth it to his sorrow; and the father of a churl hath no joy.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
22 A merry heart is a good medicine; but a broken spirit drieth the bones.
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
23 A wicked man taketh a gift out of the bosom, to pervert the ways of justice.
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
24 Wisdom is before him that hath understanding; but the eyes of a fool are in the ends of the earth.
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
25 A foolish son is vexation to his father, and bitterness to her that bore him.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
26 To punish also the righteous is not good, nor to strike the noble for their uprightness.
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
27 He that spareth his words hath knowledge; and he that husbandeth his spirit is a man of discernment.
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
28 Even a fool, when he holdeth his peace, is counted wise; and he that shutteth his lips is esteemed as a man of understanding.
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.

< Proverbs 17 >