< Micah 7 >

1 Woe is me! for I am as the last of the summer fruits, as the grape gleanings of the vintage; there is no cluster to eat; nor first-ripe fig which my soul desireth.
Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
2 The godly man is perished out of the earth, and the upright among men is no more; they all lie in wait for blood; they hunt every man his brother with a net.
Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
3 Their hands are upon that which is evil to do it diligently; the prince asketh, and the judge is ready for a reward; and the great man, he uttereth the evil desire of his soul; thus they weave it together.
Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
4 The best of them is as a brier; the most upright is worse than a thorn hedge; the day of thy watchmen, even thy visitation, is come; now shall be their perplexity.
Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
5 Trust ye not in a friend, put ye not confidence in a familiar friend; keep the doors of thy mouth from her that lieth in thy bosom.
Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
6 For the son dishonoureth the father, the daughter riseth up against her mother, the daughter-in-law against her mother-in-law; a man's enemies are the men of his own house.
Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
7 'But as for me, I will look unto the LORD; I will wait for the God of my salvation; my God will hear me.
Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
8 Rejoice not against me, O mine enemy; though I am fallen, I shall arise; though I sit in darkness, the LORD is a light unto me.
Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
9 I will bear the indignation of the LORD, because I have sinned against Him; until He plead my cause, and execute judgment for me; He will bring me forth to the light, and I shall behold His righteousness.
Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
10 Then mine enemy shall see it, and shame shall cover her; who said unto me: Where is the LORD thy God? Mine eyes shall gaze upon her; now shall she be trodden down as the mire of the streets.'
Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
11 'The day for building thy walls, even that day, shall be far removed.'
Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
12 There shall be a day when they shall come unto thee, from Assyria even to the cities of Egypt, and from Egypt even to the River, and from sea to sea, and from mountain to mountain.
Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
13 And the land shall be desolate for them that dwell therein, because of the fruit of their doings.
Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
14 Tend Thy people with Thy staff, the flock of Thy heritage, that dwell solitarily, as a forest in the midst of the fruitful field; let them feed in Bashan and Gilead, as in the days of old.
Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
15 'As in the days of thy coming forth out of the land of Egypt will I show unto him marvellous things.'
“Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
16 The nations shall see and be put to shame for all their might; they shall lay their hand upon their mouth, their ears shall be deaf.
Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
17 They shall lick the dust like a serpent; like crawling things of the earth they shall come trembling out of their close places; they shall come with fear unto the LORD our God, and shall be afraid because of Thee.
Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
18 Who is a God like unto Thee, that pardoneth the iniquity, and passeth by the transgression of the remnant of His heritage? He retaineth not His anger for ever, because He delighteth in mercy.
Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
19 He will again have compassion upon us; He will subdue our iniquities; and Thou wilt cast all their sins into the depths of the sea.
Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
20 Thou wilt show faithfulness to Jacob, mercy to Abraham, as Thou hast sworn unto our fathers from the days of old.
Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.

< Micah 7 >