< Micah 1 >

1 THE WORD of the LORD that came to Micah the Morashtite in the days of Jotham, Ahaz, and Hezekiah, kings of Judah, which he saw concerning Samaria and Jerusalem.
Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
2 Hear, ye peoples, all of you; Hearken, O earth, and all that therein is; and let the Lord GOD be witness against you, the Lord from His holy temple.
Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
3 For, behold, the LORD cometh forth out of His place, and will come down, and tread upon the high places of the earth.
Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
4 And the mountains shall be molten under Him, and the valleys shall be cleft, as wax before the fire, as waters that are poured down a steep place.
Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
5 For the transgression of Jacob is all this, and for the sins of the house of Israel. What is the transgression of Jacob? is it not Samaria? And what are the high places of Judah? are they not Jerusalem?
Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
6 Therefore I will make Samaria a heap in the field, a place for the planting of vineyards; and I will pour down the stones thereof into the valley, and I will uncover the foundations thereof.
“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
7 And all her graven images shall be beaten to pieces, and all her hires shall be burned with fire, and all her idols will I lay desolate; for of the hire of a harlot hath she gathered them, and unto the hire of a harlot shall they return.
Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
8 For this will I wail and howl, I will go stripped and naked; I will make a wailing like the jackals, and a mourning like the ostriches.
Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
9 For her wound is incurable; for it is come even unto Judah; it reacheth unto the gate of my people, even to Jerusalem.
Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
10 Tell it not in Gath, weep not at all; at Beth-le-aphrah roll thyself in the dust.
Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
11 Pass ye away, O inhabitant of Saphir, in nakedness and shame; the inhabitant of Zaanan is not come forth; the wailing of Beth-ezel shall take from you the standing-place thereof.
Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
12 For the inhabitant of Maroth waiteth anxiously for good; because evil is come down from the LORD unto the gate of Jerusalem.
Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
13 Bind the chariots to the swift steeds, O inhabitant of Lachish; she was the beginning of sin to the daughter of Zion; for the transgressions of Israel are found in thee.
Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
14 Therefore shalt thou give a parting gift to Moresheth-gath; the houses of Achzib shall be a deceitful thing unto the kings of Israel.
Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
15 I will yet bring unto thee, O inhabitant of Mareshah, him that shall possess thee; the glory of Israel shall come even unto Adullam.
Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
16 Make thee bald, and poll thee for the children of thy delight; enlarge thy baldness as the vulture; for they are gone into captivity from thee.
Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

< Micah 1 >