< Leviticus 24 >

1 And the LORD spoke unto Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 'Command the children of Israel, that they bring unto thee pure olive oil beaten for the light, to cause a lamp to burn continually.
“Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale, a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
3 Without the veil of the testimony, in the tent of meeting, shall Aaron order it from evening to morning before the LORD continually; it shall be a statute for ever throughout your generations.
Kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, mʼchihema cha msonkhano, Aaroni azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa, nthawi zonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yonse.
4 He shall order the lamps upon the pure candlestick before the LORD continually.
Aaroni ayatse nyale zimene zili pa choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri kuti zikhale zoyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova.
5 And thou shalt take fine flour, and bake twelve cakes thereof: two tenth parts of an ephah shall be in one cake.
“Mutenge ufa wosalala ndipo muphike makeke khumi ndi awiri ndipo keke iliyonse ikhale ya ufa wa makilogalamu awiri.
6 And thou shalt set them in two rows, six in a row, upon the pure table before the LORD.
Muwayike pa tebulo la golide wabwino kwambiri pamaso pa Yehova mʼmizere iwiri. Mzere uliwonse ukhale wa makeke asanu ndi imodzi.
7 And thou shalt put pure frankincense with each row, that it may be to the bread for a memorial-part, even an offering made by fire unto the LORD.
Pa mzere uliwonse muyikepo lubani wafungo lokoma kuti pamodzi ndi bulediyo akhale wachikumbutso cha nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova.
8 Every sabbath day he shall set it in order before the LORD continually; it is from the children of Israel, an everlasting covenant.
Sabata ndi sabata nthawi zonse Aaroni aziyika makeke amenewa pamaso pa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti akhale pangano lamuyaya.
9 And it shall be for Aaron and his sons; and they shall eat it in a holy place; for it is most holy unto him of the offerings of the LORD made by fire, a perpetual due.'
Chakudyacho ndi cha Aaroni ndi ana ake ndipo azidyera ku malo wopatulika chifukwa kwa iye chakudyacho ndi chopatulika kwambiri chochokera pa chopereka chopsereza cha Yehova.”
10 And the son of an Israelitish woman, whose father was an Egyptian, went out among the children of Israel; and the son of the Israelitish woman and a man of Israel strove together in the camp.
Tsiku lina munthu wina wamwamuna amene amayi ake anali Mwisraeli koma abambo ake anali Mwigupto anapita kwa Aisraeli ndipo anakangana ndi Mwisraeli wina ku msasa.
11 And the son of the Israelitish woman blasphemed the Name, and cursed; and they brought him unto Moses. And his mother's name was Shelomith, the daughter of Dibri, of the tribe of Dan.
Munthu uja ananyoza dzina la Yehova ndi kulitemberera. Choncho anabwera naye kwa Mose. Dzina la amayi ake linali Selomiti, mwana wa Dibiri, wa fuko la Dani.
12 And they put him in ward, that it might be declared unto them at the mouth of the LORD.
Anamuyika mʼndende mpaka atadziwa bwino chofuna cha Yehova.
13 And the LORD spoke unto Moses, saying:
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
14 'Bring forth him that hath cursed without the camp; and let all that heard him lay their hands upon his head, and let all the congregation stone him.
“Pita naye kunja kwa msasa munthu wotembererayo. Onse amene anamumva akutemberera asanjike manja awo pamutu pake ndipo gulu lonse la anthu limugende miyala.
15 And thou shalt speak unto the children of Israel, saying: Whosoever curseth his God shall bear his sin.
Choncho uza Aisraeli kuti, ‘Aliyense wotemberera Mulungu wake alangidwe.
16 And he that blasphemeth the name of the LORD, he shall surely be put to death; all the congregation shall certainly stone him; as well the stranger, as the home-born, when he blasphemeth the Name, shall be put to death.
Aliyense wonyoza dzina la Yehova, mlendo ngakhale mbadwa, aphedwe. Gulu lonse la anthu limuponye miyala.
17 And he that smiteth any man mortally shall surely be put to death.
“‘Ngati munthu wina aliyense achotsa moyo wa munthu mnzake, munthuyo ayenera kuphedwa.
18 And he that smiteth a beast mortally shall make it good: life for life.
Aliyense wopha chiweto cha mnzake ayenera kulipira china. Moyo kulipa moyo.
19 And if a man maim his neighbour; as he hath done, so shall it be done to him:
Ngati munthu avulaza mnzake, nayenso amuchite zomwe wachitira mnzakeyo:
20 breach for breach, eye for eye, tooth for tooth; as he hath maimed a man, so shall it be rendered unto him.
kuthyola fupa kulipira kuthyola fupa, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino. Monga momwe anavulazira mnzake, amuvulaze chimodzimodzinso.
21 And he that killeth a beast shall make it good; and he that killeth a man shall be put to death.
Aliyense wopha chiweto cha mnzake, alipire chiweto china, koma aliyense wopha munthu ayenera kuphedwa.
22 Ye shall have one manner of law, as well for the stranger, as for the home-born; for I am the LORD your God.'
Lamulo la mlendo ndi mbadwa ndi limodzi lomweli. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
23 And Moses spoke to the children of Israel, and they brought forth him that had cursed out of the camp, and stoned him with stones. And the children of Israel did as the LORD commanded Moses.
Pamenepo Mose anawuza Aisraeli zimenezi, ndipo iwo anatulutsira munthu wotembererayo kunja kwa msasa ndi kumugenda miyala. Aisraeli anachita zimene Yehova analamula Mose.

< Leviticus 24 >