< Lamentations 1 >
1 HOW DOTH the city sit solitary, that was full of people! How is she become as a widow! She that was great among the nations, and princess among the provinces, how is she become tributary!
Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha, umene kale unali wodzaza ndi anthu! Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu! Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye. Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi, tsopano wasanduka kapolo.
2 She weepeth sore in the night, and her tears are on her cheeks; she hath none to comfort her among all her lovers; all her friends have dealt treacherously with her, they are become her enemies.
Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse, misozi ili pa masaya pake. Mwa abwenzi ake onse, palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza. Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu; onse akhala adani ake.
3 Judah is gone into exile because of affliction, and because of great servitude; she dwelleth among the nations, she findeth no rest; all her pursuers overtook her within the straits.
Yuda watengedwa ku ukapolo, kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa. Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina; ndipo alibe malo opumulira. Onse omuthamangitsa iye amupitirira, ndipo alibe kwina kothawira.
4 The ways of Zion do mourn, because none come to the solemn assembly; all her gates are desolate, her priests sigh; her virgins are afflicted, and she herself is in bitterness.
Misewu yopita ku Ziyoni ikulira, chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake. Zipata zake zonse zili pululu, ansembe akubuwula. Anamwali ake akulira, ndipo ali mʼmasautso woopsa.
5 Her adversaries are become the head, her enemies are at ease; for the LORD hath afflicted her for the multitude of her transgressions; her young children are gone into captivity before the adversary.
Adani ake asanduka mabwana ake; odana naye akupeza bwino. Yehova wamubweretsera mavuto chifukwa cha machimo ake ambiri. Ana ake atengedwa ukapolo pamaso pa mdani.
6 And gone is from the daughter of Zion all her splendour; her princes are become like harts that find no pasture, and they are gone without strength before the pursuer.
Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni wachokeratu. Akalonga ake ali ngati mbawala zosowa msipu; alibe mphamvu zothawira owathamangitsa.
7 Jerusalem remembereth in the days of her affliction and of her anguish all her treasures that she had from the days of old; now that her people fall by the hand of the adversary, and none doth help her, the adversaries have seen her, they have mocked at her desolations.
Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake, Yerusalemu amakumbukira chuma chonse chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake. Anthu ake atagwidwa ndi adani ake, panalibe aliyense womuthandiza. Adani ake ankamuyangʼana ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
8 Jerusalem hath grievously sinned, therefore she is become as one unclean; all that honoured her despise her, because they have seen her nakedness; she herself also sigheth, and turneth backward.
Yerusalemu wachimwa kwambiri ndipo potero wakhala wodetsedwa. Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza, chifukwa aona umaliseche wake. Iye mwini akubuwula ndipo akubisa nkhope yake.
9 Her filthiness was in her skirts, she was not mindful of her end; therefore is she come down wonderfully, she hath no comforter. 'Behold, O LORD, my affliction, for the enemy hath magnified himself.'
Uve wake umaonekera pa zovala zake; iye sanaganizire za tsogolo lake. Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu; ndipo analibe womutonthoza. “Inu Yehova, taonani masautso anga, pakuti mdani wapambana.”
10 The adversary hath spread out his hand upon all her treasures; for she hath seen that the heathen are entered into her sanctuary, concerning whom Thou didst command that they should not enter into Thy congregation.
Adani amulanda chuma chake chonse; iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika, amene Inu Mulungu munawaletsa kulowa mu msonkhano wanu.
11 All her people sigh, they seek bread; they have given their pleasant things for food to refresh the soul. 'See, O LORD, and behold, how abject I am become.'
Anthu ake onse akubuwula pamene akufunafuna chakudya; asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya kuti akhale ndi moyo. “Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani, chifukwa ine ndanyozeka.”
12 'Let it not come unto you, all ye that pass by! Behold, and see if there be any pain like unto my pain, which is done unto me, wherewith the LORD hath afflicted me in the day of His fierce anger.
“Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa? Yangʼanani ndipo muone. Kodi pali mavuto ofanana ndi amene andigwerawa, amene Ambuye anandibweretsera pa tsiku la ukali wake?
13 From on high hath He sent fire into my bones, and it prevaileth against them; He hath spread a net for my feet, He hath turned me back; He hath made me desolate and faint all the day.
“Anatumiza moto kuchokera kumwamba, unalowa mpaka mʼmafupa anga. Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga ndipo anandibweza. Anandisiya wopanda chilichonse, wolefuka tsiku lonse.
14 The yoke of my transgressions is impressed by His hand; they are knit together, they are come up upon my neck; He hath made my strength to fail; the Lord hath delivered me into their hands, against whom I am not able to stand.
“Wazindikira machimo anga onse ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi. Machimowa afika pakhosi panga, ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu. Iye wandipereka kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
15 The Lord hath set at nought all my mighty men in the midst of me; He hath called a solemn assembly against me to crush my young men; the Lord hath trodden as in a winepress the virgin the daughter of Judah.'
“Ambuye wakana anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane: wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane, kuti litekedze anyamata anga; mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza anamwali a Yuda.
16 'For these things I weep; mine eye, mine eye runneth down with water; because the comforter is far from me, even he that should refresh my soul; my children are desolate, because the enemy hath prevailed.'
“Chifukwa cha zimenezi ndikulira ndipo maso anga adzaza ndi misozi. Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze, palibe aliyense wondilimbitsa mtima. Ana anga ali okhaokha chifukwa mdani watigonjetsa.
17 Zion spreadeth forth her hands; there is none to comfort her; the LORD hath commanded concerning Jacob, that they that are round about him should be his adversaries; Jerusalem is among them as one unclean.
“Ziyoni wakweza manja ake, koma palibe aliyense womutonthoza. Yehova walamula kuti abale ake a Yakobo akhale adani ake; Yerusalemu wasanduka chinthu chodetsedwa pakati pawo.
18 'The LORD is righteous; for I have rebelled against His word; hear, I pray you, all ye peoples, and behold my pain: my virgins and my young men are gone into captivity.
“Yehova ndi wolungama, koma ndine ndinawukira malamulo ake. Imvani inu anthu a mitundu yonse; onani masautso anga. Anyamata ndi anamwali anga agwidwa ukapolo.
19 I called for my lovers, but they deceived me; my priests and mine elders perished in the city, while they sought them food to refresh their souls.
“Ndinayitana abwenzi anga koma anandinyenga. Ansembe ndi akuluakulu anga anafa mu mzinda pamene ankafunafuna chakudya kuti akhale ndi moyo.
20 Behold, O LORD, for I am in distress, mine inwards burn; my heart is turned within me, for I have grievously rebelled. Abroad the sword bereaveth, at home there is the like of death.
“Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira! Ndikuzunzika mʼkati mwanga, ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa chifukwa ndakhala osamvera. Mʼmisewu anthu akuphedwa, ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.
21 They have heard that I sigh, there is none to comfort me; all mine enemies have heard of my trouble, and are glad, for Thou hast done it; Thou wilt bring the day that Thou hast proclaimed, and they shall be like unto me.
“Anthu amva kubuwula kwanga, koma palibe wonditonthoza. Adani anga onse amva masautso anga; iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita. Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija kuti iwonso adzakhale ngati ine.
22 Let all their wickedness come before Thee; and do unto them, as Thou hast done unto me for all my transgressions; for my sighs are many and my heart is faint.'
“Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu; muwalange ngati mmene mwandilangira ine chifukwa cha machimo anga onse. Ndikubuwula kwambiri ndipo mtima wanga walefuka.”