< Judges 18 >

1 In those days there was no king in Israel; and in those days the tribe of the Danites sought them an inheritance to dwell in; for unto that day there had nothing been allotted unto them among the tribes of Israel for an inheritance.
Masiku amenewo munalibe mfumu mu Israeli. Ndipo anthu a fuko la Dani amafunafuna malo okhalamo ngati cholowa chawo, chifukwa kufikira nthawi imeneyo anali asanalandire cholowa chawo pakati pa mafuko a Israeli.
2 And the children of Dan sent of their family five men from their whole number, men of valour, from Zorah, and from Eshtaol, to spy out the land, and to search it; and they said unto them: 'Go, search the land'; and they came to the hill-country of Ephraim, unto the house of Micah, and lodged there.
Choncho fuko la Dani linatumiza kuchokera ku mabanja awo onse anthu olimba mtima asanu. Anthuwa anachokera ku Zora ndi ku Esitaoli ndipo anatumidwa kukazonda ndi kuliyendera dzikolo. Anthu amenewa ankayimira fuko lonse la Dani. Anthuwa anawawuza kuti, “Pitani mukazonde dzikolo.” Anthuwa anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ndi kupita ku nyumba ya Mika komwe anakagona.
3 When they were by the house of Micah, they knew the voice of the young man the Levite; and they turned aside thither, and said unto him: 'Who brought thee hither? and what doest thou in this place? and what hast thou here?'
Ali ku nyumba ya Mika anazindikira mawu a mnyamata, Mlevi uja. Choncho anapita kwa iye namufunsa kuti, “Unabwera ndi ndani kuno? Nanga ukuchita chiyani ku malo ano? Komanso nʼchifukwa chiyani uli kuno?”
4 And he said unto them: 'Thus and thus hath Micah dealt with me, and he hath hired me, and I am become his priest.'
Iye anawawuza zimene Mika anamuchitira ndipo anati, “Iye anandilemba ntchito ndipo ndine wansembe wake.”
5 And they said unto him: 'Ask counsel, we pray thee, of God, that we may know whether our way which we are going shall be prosperous.'
Kenaka iwo anati kwa iye, “Chonde tifunsire kwa Mulungu kuti tidziwe ngati ulendo wathuwu tiyende bwino.”
6 And the priest said unto them: 'Go in peace; before the LORD is your way wherein ye go.'
Wansembeyo anawayankha kuti, “Pitani mu mtendere, Yehova ali ndi inu pa ulendo wanuwu.”
7 Then the five men departed, and came to Laish, and saw the people that were therein, how they dwelt in security, after the manner of the Zidonians, quiet and secure; for there was none in the land, possessing authority, that might put them to shame in any thing, and they were far from the Zidonians, and had no dealings with any man.
Choncho anthu asanuwo ananyamuka ndipo anafika ku Laisi, kumene anaona kuti anthu ankakhala mwabata monga anthu a ku Sidoni. Anali anthu opanda chowavuta ndiponso aphee. Tsono popeza mʼdziko mwawo analibe chosowa, iwo anali a chuma. Anaonanso kuti anthuwo ankakhala kutali ndi Sidoni ndipo analibe ubale ndi wina aliyense.
8 And they came unto their brethren to Zorah and Eshtaol; and their brethren said unto them: 'What say ye?'
Ozonda dziko aja atabwerera kwa abale awo ku Zora ndi Esitaoli, abale awowo anawafunsa kuti, “Mwaonako zotani?”
9 And they said: 'Arise, and let us go up against them; for we have seen the land, and, behold, it is very good; and are ye still? be not slothful to go and to enter in to possess the land.
“Tiyeni tikamenyane nawo nkhondo popeza taliona dziko lawolo kuti ndi lachonde kwambiri. Kodi simuchitapo kanthu? Musachite mphwayi kupita mʼdzikomo ndi kukalilanda.
10 When ye go, ye shall come unto a people secure, and the land is large; for God hath given it into your hand; a place where there is no want; it hath every thing that is in the earth.'
Mukalowa, mukapeza anthu amene ali osatekeseka ndi dziko lalikulu. Yehova wakupatsani dziko limeneli. Malowo ngosasowa kanthu kalikonse kopezeka pa dziko lapansi.”
11 And there set forth from thence of the family of the Danites, out of Zorah and out of Eshtaol, six hundred men girt with weapons of war.
Kenaka anthu 600 a fuko la Dani ananyamuka ku Zora ndi Esitaoli atanyamula zida za nkhondo.
12 And they went up, and encamped in Kiriath-jearim, in Judah; wherefore that place was called Mahaneh-dan unto this day; behold, it is behind Kiriath-jearim.
Tsono anakamanga msasa ku Kiriati-Yearimu mʼdziko la Yuda. Malowa ali kumadzulo kwa Kiriati-Yearimu. Ichi ndi chifukwa chake malowo akutchedwa Mahane Dani mpaka lero.
13 And they passed thence unto the hill-country of Ephraim, and came unto the house of Micah.
Kuchokera kumeneko anapita ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anafika ku nyumba ya Mika.
14 Then answered the five men that went to spy out the country of Laish, and said unto their brethren: 'Do ye know that there is in these houses an ephod, and teraphim, and a graven image, and a molten image? now therefore consider what ye have to do.'
Anthu asanu amene anakazonda dziko la Laisi anati kwa abale awo, “Kodi mukudziwa kuti imodzi mwa nyumba izi muli efodi, mafano a mʼnyumba otchedwa terafimu, fano losema ndiponso fano lokuta ndi siliva? Ndiye mudziwe chochita.”
15 And they turned aside thither, and came to the house of the young man the Levite, even unto the house of Micah, and asked him of his welfare.
Choncho anthuwa anapatuka napita ku nyumba ya Mika kumene mnyamata, Mlevi uja ankakhala ndipo anamufunsa za mmene zinthu zilili.
16 And the six hundred men girt with their weapons of war, who were of the children of Dan, stood by the entrance of the gate.
Nthawi imeneyi nʼkuti anthu 600 a fuko la Dani aja atayima pa chipata atanyamula zida za nkhondo.
17 And the five men that went to spy out the land went up, and came in thither, and took the graven image, and the ephod, and the teraphim, and the molten image; and the priest stood by the entrance of the gate with the six hundred men girt with weapons of war.
Anthu asanu amene anakazonda dziko aja analowa ndi kukatenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba lotchedwa terafimu, ndi fano lokutidwa ndi siliva. Nthawiyi nʼkuti wansembe uja ndi anthu 600 okhala ndi zida za nkhondo aja ali chiyimire pa chipata.
18 And when these went into Micah's house, and fetched the graven image of the ephod, and the teraphim, and the molten image, the priest said unto them: 'What do ye?'
Anthuwo atalowa mʼnyumba ya Mika ndi kutenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba, ndi fano lokutidwa ndi siliva, wansembeyo anawafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
19 And they said unto him: 'Hold thy peace, lay thy hand upon thy mouth, and go with us, and be to us a father and a priest; is it better for thee to be priest unto the house of one man, or to be priest unto a tribe and a family in Israel?'
Iwo anamuyankha kuti, “Khala chete usayankhule. Tsagana nafe ndipo udzakhala mlangizi wathu ndi wansembe wathu. Kodi si kwabwino kwa iwe kukhala wansembe wa fuko lonse la Israeli mʼmalo mokhala wansembe wa munthu mmodzi yekha?”
20 And the priest's heart was glad, and he took the ephod, and the teraphim, and the graven image, and went in the midst of the people.
Wansembeyo anakondwera ndipo anatenga efodi, fano la mʼnyumba ndi fano losema natsagana nawo.
21 So they turned and departed, and put the little ones and the cattle and the goods before them.
Choncho iwo anatembenuka nachoka, atatsogoza ana, zoweta ndi katundu wawo yense.
22 When they were a good way from the house of Micah, the men that were in the houses near to Micah's house were gathered together, and overtook the children of Dan.
Atayenda mtunda pangʼono kuchokera pa nyumba ya Mika, anthu amene amakhala pafupi ndi nyumba ya Mika anasonkhana kulondola a fuko la Dani aja, ndipo anawapeza.
23 And they cried unto the children of Dan. And they turned their faces, and said unto Micah: 'What aileth thee, that thou comest with such a company?'
Atawafuwulira, a fuko la Dani aja anachewuka ndipo anafunsa Mika kuti, “Chavuta nʼchiyani kuti usonkhanitse anthu chotere?”
24 And he said: 'Ye have taken away my god which I made, and the priest, and are gone away, and what have I more? and how then say ye unto me: What aileth thee?'
Iye anayankha kuti, “Inu mwanditengera milungu imene ndinapanga pamodzi ndi wansembe nʼkumapita. Tsono ine ndatsala ndi chiyani? Ndiye inu mungafunse kuti chavuta nʼchiyani?”
25 And the children of Dan said unto him: 'Let not thy voice be heard among us, lest angry fellows fall upon you, and thou lose thy life, with the lives of thy household.'
Anthu a fuko la Dani aja anayankha kuti, “Usayankhuleponso kanthu chifukwa anthu awa angapse mtima nakumenya ndipo iwe ndi banja lako lonse nʼkutayapo miyoyo yanu.”
26 And the children of Dan went their way; and when Micah saw that they were too strong for him, he turned and went back unto his house.
Choncho anthu a fuko la Dani anapitiriza ulendo wawo. Mika ataona kuti anthuwo anali amphamvu kuposa iye, anangotembenuka kubwerera kwawo.
27 And they took that which Micah had made, and the priest whom he had, and came unto Laish, unto a people quiet and secure, and smote them with the edge of the sword; and they burnt the city with fire.
Anthu a fuko la Dani aja anatenga zinthu zimene Mika anapanga pamodzi ndi wansembe uja. Iwo anakafika ku Laisi kwa anthu a phee, osatekeseka aja ndipo anawathira nkhondo, nawapha ndi kutentha mzindawo ndi moto.
28 And there was no deliverer, because it was far from Zidon, and they had no dealings with any man; and it was in the valley that lieth by Beth-rehob. And they built the city, and dwelt therein.
Panalibe wowapulumutsa chifukwa anali kutali ndi Sidoni ndiponso sanali pa ubale ndi wina aliyense. Mzindawo unali mʼchigwa cha Beti-Rehobu. Anthu a fuko la Adaniwo anawumanganso mzindawo ndi kumakhalamo.
29 And they called the name of the city Dan, after the name of Dan their father, who was born unto Israel; howbeit the name of the city was Laish at the first.
Iwo anawutcha mzindawo Dani, kutengera dzina la kholo lawo Dani, amene anali mwana wa Israeli, ngakhale kuti mzindawo poyamba unali Laisi.
30 And the children of Dan set up for themselves the graven image; and Jonathan, the son of Gershom, the son of Manasseh, he and his sons were priests to the tribe of the Danites until the day of the captivity of the land.
Anthu a fuko la Dani anayimiritsa fano losema lija. Yonatani mwana wa Geresomu, mwana wa Mose pamodzi ndi ana ake onse anakhala ansembe a fuko la Dani mpaka pa tsiku la ukapolo wa dzikolo.
31 So they set them up Micah's graven image which he made, all the time that the house of God was in Shiloh.
Choncho anthu a fuko la Dani ankapembedza fano limene Mika anapanga nthawi yonse pamene nyumba ya Mulungu inali ku Silo.

< Judges 18 >