< Jonah 3 >

1 And the word of the LORD came unto Jonah the second time, saying:
Ndipo Yehova anayankhula ndi Yona kachiwiri kuti,
2 'Arise, go unto Nineveh, that great city, and make unto it the proclamation that I bid thee.'
“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire uthenga umene ndikupatsa.”
3 So Jonah arose, and went unto Nineveh, according to the word of the LORD. Now Nineveh was an exceeding great city, of three days' journey.
Yona anamvera mawu a Yehova ndipo anapita ku Ninive. Tsono Ninive unali mzinda waukulu kwambiri; wofunika masiku atatu kuwudutsa.
4 And Jonah began to enter into the city a day's journey, and he proclaimed, and said: 'Yet forty days, and Nineveh shall be overthrown.'
Yona analowa mu mzindawo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi. Iye ankalalikira kuti, “Atsala masiku makumi anayi kuti Ninive awonongedwe.”
5 And the people of Nineveh believed God; and they proclaimed a fast, and put on sackcloth, from the greatest of them even to the least of them.
Anthu a ku Ninive anakhulupirira Mulungu. Analengeza kuti aliyense, wamkulu ndi wamngʼono yemwe asale zakudya ndipo avale chiguduli.
6 And the tidings reached the king of Nineveh, and he arose from his throne, and laid his robe from him, and covered him with sackcloth, and sat in ashes.
Mfumu ya ku Ninive itamva nkhaniyi, inatsika pa mpando wake waufumu, nivula mkanjo wake waufumu ndipo inavala chiguduli ndi kukhala pansi pa fumbi.
7 And he caused it to be proclaimed and published through Nineveh by the decree of the king and his nobles, saying: 'Let neither man nor beast, herd nor flock, taste any thing; let them not feed, nor drink water;
Tsono mfumuyo inalengeza mu Ninive kuti, “Mwa lamulo lochokera kwa mfumu ndi akalonga ake: “Munthu aliyense kapenanso nyama, ngʼombe kapena nkhosa, zisadye kanthu kalikonse; musazilole kuti zidye kapena kumwa.
8 but let them be covered with sackcloth, both man and beast, and let them cry mightily unto God; yea, let them turn every one from his evil way, and from the violence that is in their hands.
Koma anthu avale ziguduli, ndipo nyamanso aziveke ziguduli. Munthu aliyense azifuwula kwa Mulungu ndi mphamvu zake zonse. Anthuwo asiye makhalidwe awo oyipa ndi machitidwe achiwawa.
9 Who knoweth whether God will not turn and repent, and turn away from His fierce anger, that we perish not?'
Angadziwe ndani? Mwina Mulungu nʼkutikhululukira ndipo mwa chifundo chake nʼkuleka kutikwiyira, ifeyo osawonongedwa.”
10 And God saw their works, that they turned from their evil way; and God repented of the evil, which He said He would do unto them; and He did it not.
Mulungu ataona zimene anthuwo anachita, ndi mmene anasiyira makhalidwe awo oyipa, anawachitira chifundo ndipo sanabweretse chiwonongeko chimene anawaopseza nacho.

< Jonah 3 >