< Job 9 >

1 Then Job answered and said:
Ndipo Yobu anayankha kuti,
2 Of a truth I know that it is so; and how can man be just with God?
“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
3 If one should desire to contend with Him, he could not answer Him one of a thousand.
Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
4 He is wise in heart, and mighty in strength; who hath hardened himself against Him, and prospered?
Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
5 Who removeth the mountains, and they know it not, when He overturneth them in His anger.
Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
6 Who shaketh the earth out of her place, and the pillars thereof tremble.
Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
7 Who commandeth the sun, and it riseth not; and sealeth up the stars.
Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
8 Who alone stretcheth out the heavens, and treadeth upon the waves of the sea.
Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
9 Who maketh the Bear, Orion, and the Pleiades, and the chambers of the south.
Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
10 Who doeth great things past finding out; yea, marvellous things without number.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
11 Lo, He goeth by me, and I see Him not. He passeth on also, but I perceive Him not.
Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
12 Behold, He snatcheth away, who can hinder Him? Who will say unto Him: 'What doest Thou?'
Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
13 God will not withdraw His anger; the helpers of Rahab did stoop under Him.
Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
14 How much less shall I answer Him, and choose out my arguments with Him?
“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
15 Whom, though I were righteous, yet would I not answer; I would make supplication to Him that contendeth with me.
Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
16 If I had called, and He had answered me; yet would I not believe that He would hearken unto my voice —
Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
17 He that would break me with a tempest, and multiply my wounds without cause;
Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
18 That would not suffer me to take my breath, but fill me with bitterness.
Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
19 If it be a matter of strength, lo, He is mighty! and if of justice, who will appoint me a time?
Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
20 Though I be righteous, mine own mouth shall condemn me; though I be innocent, He shall prove me perverse.
Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
21 I am innocent — I regard not myself, I despise my life.
“Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
22 It is all one — therefore I say: He destroyeth the innocent and the wicked.
Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
23 If the scourge slay suddenly, He will mock at the calamity of the guiltless.
Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
24 The earth is given into the hand of the wicked; he covereth the faces of the judges thereof; if it be not He, who then is it?
Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
25 Now my days are swifter than a runner; they flee away, they see no good.
“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
26 They are passed away as the swift ships; as the vulture that swoopeth on the prey.
Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
27 If I say: 'I will forget my complaint, I will put off my sad countenance, and be of good cheer',
Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
28 I am afraid of all my pains, I know that Thou wilt not hold me guiltless.
ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
29 I shall be condemned; why then do I labour in vain?
Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
30 If I wash myself with snow water, and make my hands never so clean;
Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
31 Yet wilt Thou plunge me in the ditch, and mine own clothes shall abhor me.
mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
32 For He is not a man, as I am, that I should answer Him, that we should come together in judgment.
“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
33 There is no arbiter betwixt us, that might lay his hand upon us both.
Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
34 Let Him take His rod away from me, and let not His terror make me afraid;
munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
35 Then would I speak, and not fear Him; for I am not so with myself.
Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.

< Job 9 >