< Job 40 >
1 Moreover the LORD answered Job, and said:
Yehova anati kwa Yobu:
2 Shall he that reproveth contend with the Almighty? He that argueth with God, let him answer it.
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Then Job answered the LORD, and said:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 Behold, I am of small account; what shall I answer Thee? I lay my hand upon my mouth.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Once have I spoken, but I will not answer again; yea, twice, but I will proceed no further.
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Then the LORD answered Job out of the whirlwind, and said:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 Gird up thy loins now like a man; I will demand of thee, and declare thou unto Me.
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Wilt thou even make void My judgment? Wilt thou condemn Me, that thou mayest be justified?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Or hast thou an arm like God? And canst thou thunder with a voice like Him?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Deck thyself now with majesty and excellency, and array thyself with glory and beauty.
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Cast abroad the rage of thy wrath; and look upon every one that is proud, and abase him.
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Look on every one that is proud, and bring him low; and tread down the wicked in their place.
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Hide them in the dust together; bind their faces in the hidden place.
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Then will I also confess unto thee that thine own right hand can save thee.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Behold now behemoth, which I made with thee; he eateth grass as an ox.
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Lo now, his strength is in his loins, and his force is in the stays of his body.
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 He straineth his tail like a cedar; the sinews of his thighs are knit together.
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 His bones are as pipes of brass; his gristles are like bars of iron.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 He is the beginning of the ways of God; He only that made him can make His sword to approach unto him.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 Surely the mountains bring him forth food, and all the beasts of the field play there.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 He lieth under the lotus-trees, in the covert of the reed, and fens.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 The lotus-trees cover him with their shadow; the willows of the brook compass him about.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Behold, if a river overflow, he trembleth not; he is confident, though the Jordan rush forth to his mouth.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Shall any take him by his eyes, or pierce through his nose with a snare?
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?