< Job 39 >

1 Knowest thou the time when the wild goats of the rock bring forth? Or canst thou mark when the hinds do calve?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 Canst thou number the months that they fulfil? Or knowest thou the time when they bring forth?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 They bow themselves, they bring forth their young, they cast out their fruit.
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Their young ones wax strong, they grow up in the open field; they go forth, and return not again.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Who hath sent out the wild ass free? Or who hath loosed the bands of the wild ass?
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 Whose house I have made the wilderness, and the salt land his dwelling-place.
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 He scorneth the tumult of the city, neither heareth he the shoutings of the driver.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 The range of the mountains is his pasture, and he searcheth after every green thing.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Will the wild-ox be willing to serve thee? Or will he abide by thy crib?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Canst thou bind the wild-ox with his band in the furrow? Or will he harrow the valleys after thee?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Wilt thou trust him, because his strength is great? Or wilt thou leave thy labour to him?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Wilt thou rely on him, that he will bring home thy seed, and gather the corn of thy threshing-floor?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 The wing of the ostrich beateth joyously; but are her pinions and feathers the kindly stork's?
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 For she leaveth her eggs on the earth, and warmeth them in dust,
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 And forgetteth that the foot may crush them, or that the wild beast may trample them.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 She is hardened against her young ones, as if they were not hers; though her labour be in vain, she is without fear;
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Because God hath deprived her of wisdom, neither hath He imparted to her understanding.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 When the time cometh, she raiseth her wings on high, and scorneth the horse and his rider.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 Hast thou given the horse his strength? Hast thou clothed his neck with fierceness?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Hast thou made him to leap as a locust? The glory of his snorting is terrible.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 He paweth in the valley, and rejoiceth in his strength; he goeth out to meet the clash of arms.
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 He mocketh at fear, and is not affrighted; neither turneth he back from the sword.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 The quiver rattleth upon him, the glittering spear and the javelin.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 He swalloweth the ground with storm and rage; neither believeth he that it is the voice of the horn.
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 As oft as he heareth the horn he saith: 'Ha, ha!' and he smelleth the battle afar off, the thunder of the captains, and the shouting.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Doth the hawk soar by thy wisdom, and stretch her wings toward the south?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Doth the vulture mount up at thy command, and make her nest on high?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 She dwelleth and abideth on the rock, upon the crag of the rock, and the stronghold.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 From thence she spieth out the prey; her eyes behold it afar off.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Her young ones also suck up blood; and where the slain are, there is she.
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”

< Job 39 >