< Job 36 >
1 Elihu also proceeded, and said:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Suffer me a little, and I will tell thee; for there are yet words on God's behalf.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 I will fetch my knowledge from afar, and will ascribe righteousness to my Maker.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 For truly my words are not false; one that is upright in mind is with thee.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Behold, God is mighty, yet He despiseth not any; He is mighty in strength of understanding.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 He preserveth not the life of the wicked; but giveth to the poor their right.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 He withdraweth not His eyes from the righteous; but with kings upon the throne He setteth them for ever, and they are exalted.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 And if they be bound in fetters, and be holden in cords of affliction;
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 Then He declareth unto them their work, and their transgressions, that they have behaved themselves proudly.
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 He openeth also their ear to discipline, and commandeth that they return from iniquity.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 If they hearken and serve Him, they shall spend their days in prosperity, and their years in pleasures.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 But if they hearken not, they shall perish by the sword, and they shall die without knowledge.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 But they that are godless in heart lay up anger; they cry not for help when He bindeth them.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Their soul perisheth in youth, and their life as that of the depraved.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 He delivereth the afflicted by His affliction, and openeth their ear by tribulation.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Yea, He hath allured thee out of distress into a broad place, where there is no straitness; and that which is set on thy table is full of fatness;
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 And thou art full of the judgment of the wicked; judgment and justice take hold on them.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 For beware of wrath, lest thou be led away by thy sufficiency; neither let the greatness of the ransom turn thee aside.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Will thy riches avail, that are without stint, or all the forces of thy strength?
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Desire not the night, when peoples are cut off in their place.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Take heed, regard not iniquity; for this hast thou chosen rather than affliction.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Behold, God doeth loftily in His power; who is a teacher like Him?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Who hath enjoined Him His way? Or who hath said: 'Thou hast wrought unrighteousness'?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Remember that thou magnify His work, whereof men have sung.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 All men have looked thereon; man beholdeth it afar off.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Behold, God is great, beyond our knowledge; the number of His years is unsearchable.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 For He draweth away the drops of water, which distil rain from His vapour;
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Which the skies pour down and drop upon the multitudes of men.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Yea, can any understand the spreadings of the clouds, the crashings of His pavilion?
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Behold, He spreadeth His light upon it; and He covereth the depths of the sea.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 For by these He judgeth the peoples; He giveth food in abundance.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 He covereth His hands with the lightning, and giveth it a charge that it strike the mark.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 The noise thereof telleth concerning it, the cattle also concerning the storm that cometh up.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.