< Job 35 >
1 Moreover Elihu answered and said:
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 Thinkest thou this to be thy right, or sayest thou: 'I am righteousness before God',
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 That thou inquirest: 'What advantage will it be unto Thee?' And: 'What profit shall I have, more than if I had sinned?'
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 I will give thee answer, and thy companions with thee.
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Look unto the heavens, and see; and behold the skies, which are higher than thou.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 If thou hast sinned, what doest thou against Him? And if thy transgressions be multiplied, what doest thou unto Him?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 If thou be righteous, what givest thou Him? Or what receiveth He of thy hand?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 Thy wickedness concerneth a man as thou art; and thy righteousness a son of man.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 By reason of the multitude of oppressions they cry out; they cry for help by reason of the arm of the mighty.
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 But none saith: 'Where is God my Maker, who giveth songs in the night;
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 Who teacheth us more than the beasts of the earth, and maketh us wiser than the fowls of heaven?'
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 There they cry, but none giveth answer, because of the pride of evil men.
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Surely God will not hear vanity, neither will the Almighty regard it.
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Yea, when thou sayest thou canst not see Him — the cause is before Him; therefore wait thou for Him.
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 And now, is it for nought that He punished in His anger? And hath He not full knowledge of arrogance?
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 But Job doth open his mouth in vanity; he multiplieth words without knowledge.
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”