< Job 33 >

1 Howbeit, Job, I pray thee, hear my speech, and hearken to all my words.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Behold now, I have opened my mouth, my tongue hath spoken in my mouth.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 My words shall utter the uprightness of my heart; and that which my lips know they shall speak sincerely.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 The spirit of God hath made me, and the breath of the Almighty given me life.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 If thou canst, answer thou me, set thy words in order before me, stand forth.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Behold, I am toward God even as thou art; I also am formed out of the clay.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Behold, my terror shall not make thee afraid, neither shall my pressure be heavy upon thee.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 Surely thou hast spoken in my hearing, and I have heard the voice of thy words;
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 'I am clean, without transgression, I am innocent, neither is there iniquity in me;
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Behold, He findeth occasions against me, He counteth me for His enemy;
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 He putteth my feet in the stocks, He marketh all my paths.'
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Behold, I answer thee: In this thou art not right, that God is too great for man;
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Why hast thou striven against Him? seeing that He will not answer any of his words.
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 For God speaketh in one way, yea in two, though man perceiveth it not.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 In a dream, in a vision of the night, when deep sleep falleth upon men, in slumberings upon the bed;
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Then He openeth the ears of men, and by their chastisement sealeth the decree,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 That men may put away their purpose, and that He may hide pride from man;
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 That He may keep back his soul from the pit, and his life from perishing by the sword.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 He is chastened also with pain upon his bed, and all his bones grow stiff;
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 So that his life maketh him to abhor bread, and his soul dainty food.
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 His flesh is consumed away, that it cannot be seen; and his bones corrode to unsightliness.
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 Yea, his soul draweth near unto the pit, and his life to the destroyers.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 If there be for him an angel, an intercessor, one among a thousand, to vouch for a man's uprightness;
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 Then He is gracious unto him, and saith: 'Deliver him from going down to the pit, I have found a ransom.'
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 His flesh is tenderer than a child's; he returneth to the days of his youth;
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 He prayeth unto God, and He is favourable unto him; so that he seeth His face with joy; and He restoreth unto man his righteousness.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 He cometh before men, and saith: 'I have sinned, and perverted that which was right, and it profited me not.'
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 So He redeemeth his soul from going into the pit, and his life beholdeth the light.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Lo, all these things doth God work, twice, yea thrice, with a man,
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 To bring back his soul from the pit, that he may be enlightened with the light of the living.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Mark well, O Job, hearken unto me; hold thy peace, and I will speak.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 If thou hast any thing to say, answer me; speak, for I desire to justify thee.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 If not, hearken thou unto me; hold thy peace, and I will teach thee wisdom.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Job 33 >