< Job 32 >

1 So these three men ceased to answer Job, because he was righteous in his own eyes.
Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
2 Then was kindled the wrath of Elihu the son of Barachel the Buzite, of the family of Ram; against Job was his wrath kindled, because he justified himself rather than God.
Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
3 Also against his three friends was his wrath kindled, because they had found no answer, and yet had condemned Job.
Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
4 Now Elihu had waited to speak unto Job, because they were older than he.
Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
5 And when Elihu saw that there was no answer in the mouth of these three men, his wrath was kindled.
Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
6 And Elihu the son of Barachel the Buzite answered and said: I am young, and ye are very old; wherefore I held back, and durst not declare you mine opinion.
Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
7 I said: 'Days should speak, and multitude of years should teach wisdom.'
Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
8 But it is a spirit in man, and the breath of the Almighty, that giveth them understanding.
Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
9 It is not the great that are wise, nor the aged that discern judgment.
Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
10 Therefore I say: 'Hearken to me; I also will declare mine opinion.'
“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
11 Behold, I waited for your words, I listened for your reasons, whilst ye searched out what to say.
Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
12 Yea, I attended unto you, and, behold, there was none that convinced Job, or that answered his words, among you.
ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
13 Beware lest ye say: 'We have found wisdom; God may vanquish him, not man!'
Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
14 For he hath not directed his words against me; neither will I answer him with your speeches.
Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
15 They are amazed, they answer no more; words are departed from them.
“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
16 And shall I wait, because they speak not, because they stand still, and answer no more?
Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
17 I also will answer my part, I also will declare mine opinion.
Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
18 For I am full of words; the spirit within me constraineth me.
Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
19 Behold, mine inwards are as wine which hath no vent; like new wine-skins which are ready to burst.
mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
20 I will speak, that I may find relief; I will open my lips and answer.
Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
21 Let me not, I pray you, respect any man's person; neither will I give flattering titles unto any man.
Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
22 For I know not to give flattering titles; else would my Maker soon take me away.
pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”

< Job 32 >