< Job 31 >
1 I made a covenant with mine eyes; how then should I look upon a maid?
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 For what would be the portion of God from above, and the heritage of the Almighty from on high?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 Is it not calamity to the unrighteous, and disaster to the workers of iniquity?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 Doth not He see my ways, and count all my steps?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 If I have walked with vanity, and my foot hath hasted to deceit —
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 Let me be weighed in a just balance, that God may know mine integrity —
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 If my step hath turned out of the way, and my heart walked after mine eyes, and if any spot hath cleaved to my hands;
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 Then let me sow, and let another eat; yea, let the produce of my field be rooted out.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 If my heart have been enticed unto a woman, and I have lain in wait at my neighbour's door;
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 Then let my wife grind unto another, and let others bow down upon her.
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 For that were a heinous crime; yea, it were an iniquity to be punished by the judges.
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 For it is a fire that consumeth unto destruction, and would root out all mine increase.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 If I did despise the cause of my man-servant, or of my maid-servant, when they contended with me —
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 What then shall I do when God riseth up? And when He remembereth, what shall I answer Him?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 Did not He that made me in the womb make him? And did not One fashion us in the womb?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 If I have withheld aught that the poor desired, or have caused the eyes of the widow to fail;
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 Or have eaten my morsel myself alone, and the fatherless hath not eaten thereof —
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 Nay, from my youth he grew up with me as with a father, and I have been her guide from my mother's womb.
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 If I have seen any wanderer in want of clothing, or that the needy had no covering;
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 If his loins have not blessed me, and if he were not warmed with the fleece of my sheep;
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 If I have lifted up my hand against the fatherless, because I saw my help in the gate;
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 Then let my shoulder fall from the shoulder-blade, and mine arm be broken from the bone.
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 For calamity from God was a terror to me, and by reason of His majesty I could do nothing.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 If I have made gold my hope, and have said to the fine gold: 'Thou art my confidence';
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 If I rejoiced because my wealth was great, and because my hand had gotten much;
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 If I beheld the sun when it shined, or the moon walking in brightness;
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 And my heart hath been secretly enticed, and my mouth hath kissed my hand;
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 This also were an iniquity to be punished by the judges; for I should have lied to God that is above.
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 If I rejoiced at the destruction of him that hated me, or exulted when evil found him —
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 Yea, I suffered not my mouth to sin by asking his life with a curse.
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 If the men of my tent said not: 'Who can find one that hath not been satisfied with his meat?'
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 The stranger did not lodge in the street; my doors I opened to the roadside.
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 If after the manner of men I covered my transgressions, by hiding mine iniquity in my bosom —
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 Because I feared the great multitude, and the most contemptible among families terrified me, so that I kept silence, and went not out of the door.
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 Oh that I had one to hear me! — Lo, here is my signature, let the Almighty answer me — and that I had the indictment which mine adversary hath written!
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Surely I would carry it upon my shoulder; I would bind it unto me as a crown.
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 I would declare unto him the number of my steps; as a prince would I go near unto him.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 If my land cry out against me, and the furrows thereof weep together;
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 If I have eaten the fruits thereof without money, or have caused the tillers thereof to be disappointed —
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 Let thistles grow instead of wheat, and noisome weeds instead of barley. The words of Job are ended.
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.