< Job 24 >

1 Why are times not laid up by the Almighty? And why do not they that know Him see His days?
“Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze? Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?
2 There are that remove the landmarks; they violently take away flocks, and feed them.
Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo; amadyetsa ziweto zimene aba.
3 They drive away the ass of the fatherless, they take the widow's ox for a pledge.
Amalanda abulu a ana amasiye ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.
4 They turn the needy out of the way; the poor of the earth hide themselves together.
Amachotsa mʼmisewu anthu osauka, ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.
5 Behold, as wild asses in the wilderness they go forth to their work, seeking diligently for food; the desert yieldeth them bread for their children.
Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu, amayendayenda kufuna chakudya; dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.
6 They cut his provender in the field; and they despoil the vineyard of the wicked.
Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake, ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.
7 They lie all night naked without clothing, and have no covering in the cold.
Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala; pa nthawi yozizira amasowa chofunda.
8 They are wet with the showers of the mountains, and embrace the rock for want of a shelter.
Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.
9 There are that pluck the fatherless from the breast, and take a pledge of the poor;
Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere; ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.
10 So that they go about naked without clothing, and being hungry they carry the sheaves;
Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala; amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.
11 They make oil within the rows of these men; they tread their winepresses, and suffer thirst.
Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa; amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.
12 From out of the populous city men groan, and the soul of the wounded crieth out; yet God imputeth it not for unseemliness.
Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda, anthu ovulala akulirira chithandizo. Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.
13 These are of them that rebel against the light; they know not the ways thereof, nor abide in the paths thereof.
“Pali ena amene amakana kuwala, amene safuna kuyenda mʼkuwalako kapena kukhala mʼnjira zake.
14 The murderer riseth with the light, to kill the poor and needy; and in the night he is as a thief.
Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka ndipo amakapha osauka ndi amphawi; nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.
15 The eye also of the adulterer waiteth for the twilight, saying: 'No eye shall see me'; and he putteth a covering on his face.
Munthu wachigololo amadikira chisisira; iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’ ndipo amaphimba nkhope yake.
16 In the dark they dig through houses; they shut themselves up in the day-time; they know not the light.
Mbala zimathyola nyumba usiku, koma masana zimadzitsekera; izo zimathawa kuwala.
17 For the shadow of death is to all of them as the morning; for they know the terrors of the shadow of death.
Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera. Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.
18 He is swift upon the face of the waters; their portion is cursed in the earth; he turneth not by the way of the vineyards.
“Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi; minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.
19 Drought and heat consume the snow waters; so doth the nether-world those that have sinned. (Sheol h7585)
Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa. (Sheol h7585)
20 The womb forgetteth him; the worm feedeth sweetly on him; he shall be no more remembered; and unrighteousness is broken as a tree.
Mayi wowabereka amawayiwala, mphutsi zimasangalala powadya; anthu oyipa sakumbukiridwanso koma amathyoka ngati mtengo.
21 He devoureth the barren that beareth not; and doeth not good to the widow.
Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana, ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.
22 He draweth away the mighty also by his power; he riseth up, and he trusteth not his own life.
Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake; ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.
23 Though it be given him to be in safety, whereon he resteth, yet His eyes are upon their ways.
Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka, koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.
24 They are exalted for a little while, and they are gone; yea, they are brought low, they are gathered in as all others, and wither as the tops of the ears of corn.
Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso; amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse; amadulidwa ngati ngala za tirigu.
25 And if it be not so now, who will prove me a liar, and make my speech nothing worth?
“Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”

< Job 24 >