< Job 18 >

1 Then answered Bildad the Shuhite, and said:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 How long will ye lay snares for words? Consider, and afterwards we will speak.
“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
3 Wherefore are we counted as beasts, and reputed dull in your sight?
Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
4 Thou that tearest thyself in thine anger, shall the earth be forsaken for thee? Or shall the rock be removed out of its place?
Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
5 Yea, the light of the wicked shall be put out, and the spark of his fire shall not shine.
“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
6 The light shall be dark in his tent, and his lamp over him shall be put out.
Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
7 The steps of his strength shall be straitened, and his own counsel shall cast him down.
Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
8 For he is cast into a net by his own feet, and he walketh upon the toils.
Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
9 A gin shall take him by the heel, and a snare shall lay hold on him.
Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 A noose is hid for him in the ground, and a trap for him in the way.
Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
11 Terrors shall overwhelm him on every side, and shall entrap him at his feet.
Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 His trouble shall be ravenous, and calamity shall be ready for his fall.
Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
13 It shall devour the members of his body, yea, the first-born of death shall devour his members.
Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 That wherein he trusteth shall be plucked out of his tent; and he shall be brought to the king of terrors.
Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 There shall dwell in his tent that which is none of his; brimstone shall be scattered upon his habitation.
Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 His roots shall dry up beneath, and above shall his branch wither.
Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
17 His remembrance shall perish from the earth, and he shall have no name abroad.
Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 He shall be driven from light into darkness, and chased out of the world.
Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 He shall have neither son nor son's son among his people, nor any remaining in his dwellings.
Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 They that come after shall be astonished at his day, as they that went before are affrighted.
Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Surely such are the dwellings of the wicked, and this is the place of him that knoweth not God.
Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

< Job 18 >