< Jeremiah 7 >

1 The word that came to Jeremiah from the LORD, saying:
Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
2 Stand in the gate of the LORD'S house, and proclaim there this word, and say: Hear the word of the LORD, all ye of Judah, that enter in at these gates to worship the LORD.
“Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
3 Thus saith the LORD of hosts, the God of Israel: Amend your ways and your doings, and I will cause you to dwell in this place.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
4 Trust ye not in lying words, saying: 'The temple of the LORD, the temple of the LORD, the temple of the LORD, are these.'
Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
5 Nay, but if ye thoroughly amend your ways and your doings; if ye thoroughly execute justice between a man and his neighbour;
Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
6 if ye oppress not the stranger, the fatherless, and the widow, and shed not innocent blood in this place, neither walk after other gods to your hurt;
ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
7 then will I cause you to dwell in this place, in the land that I gave to your fathers, for ever and ever.
Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
8 Behold, ye trust in lying words, that cannot profit.
Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
9 Will ye steal, murder, and commit adultery, and swear falsely, and offer unto Baal, and walk after other gods whom ye have not known,
“Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
10 and come and stand before Me in this house, whereupon My name is called, and say: 'We are delivered', that ye may do all these abominations?
ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
11 Is this house, whereupon My name is called, become a den of robbers in your eyes? Behold, I, even I, have seen it, saith the LORD.
Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
12 For go ye now unto My place which was in Shiloh, where I caused My name to dwell at the first, and see what I did to it for the wickedness of My people Israel.
“‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
13 And now, because ye have done all these works, saith the LORD, and I spoke unto you, speaking betimes and often, but ye heard not, and I called you, but ye answered not;
Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
14 therefore will I do unto the house, whereupon My name is called, wherein ye trust, and unto the place which I gave to you and to your fathers, as I have done to Shiloh.
choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
15 And I will cast you out of My sight, as I have cast out all your brethren, even the whole seed of Ephraim.
Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
16 Therefore pray not thou for this people, neither lift up cry nor prayer for them, neither make intercession to Me; for I will not hear thee.
“Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
17 Seest thou not what they do in the cities of Judah and in the streets of Jerusalem?
Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
18 The children gather wood, and the fathers kindle the fire, and the women knead the dough, to make cakes to the queen of heaven, and to pour out drink-offerings unto other gods, that they may provoke Me.
Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
19 Do they provoke Me? saith the LORD; do they not provoke themselves, to the confusion of their own faces?
Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
20 Therefore thus saith the Lord GOD: Behold, Mine anger and My fury shall be poured out upon this place, upon man, and upon beast, and upon the trees of the field, and upon the fruit of the land; and it shall burn, and shall not be quenched.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
21 Thus saith the LORD of hosts, the God of Israel: Add your burnt-offerings unto your sacrifices, and eat ye flesh.
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
22 For I spoke not unto your fathers, nor commanded them in the day that I brought them out of the land of Egypt, concerning burnt-offerings or sacrifices;
Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
23 but this thing I commanded them, saying: 'Hearken unto My voice, and I will be your God, and ye shall be My people; and walk ye in all the way that I command you, that it may be well with you.'
koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
24 But they hearkened not, nor inclined their ear, but walked in their own counsels, even in the stubbornness of their evil heart, and went backward and not forward,
Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
25 even since the day that your fathers came forth out of the land of Egypt unto this day; and though I have sent unto you all My servants the prophets, sending them daily betimes and often,
Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
26 yet they hearkened not unto Me, nor inclined their ear, but made their neck stiff; they did worse than their fathers.
Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
27 And thou shalt speak all these words unto them, but they will not hearken to thee; thou shalt also call unto them, but they will not answer thee.
“Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
28 Therefore thou shalt say unto them: This is the nation that hath not hearkened to the voice of the LORD their God, nor received correction; faithfulness is perished, and is cut off from their mouth.
Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
29 Cut off thy hair, and cast it away, and take up a lamentation on the high hills; for the LORD hath rejected and forsaken the generation of His wrath.
“Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
30 For the children of Judah have done that which is evil in My sight, saith the LORD; they have set their detestable things in the house whereon My name is called, to defile it.
“Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
31 And they have built the high places of Topheth, which is in the valley of the son of Hinnom, to burn their sons and their daughters in the fire; which I commanded not, neither came it into My mind.
Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
32 Therefore, behold, the days come, saith the LORD, that it shall no more be called Topheth, nor The valley of the son of Hinnom, but The valley of slaughter; for they shall bury in Topheth, for lack of room.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
33 And the carcasses of this people shall be food for the fowls of the heaven, and for the beasts of the earth; and none shall frighten them away.
Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
34 Then will I cause to cease from the cities of Judah, and from the streets of Jerusalem, the voice of mirth and the voice of gladness, the voice of the bridegroom and the voice of the bride; for the land shall be desolate.
Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”

< Jeremiah 7 >