< Jeremiah 43 >

1 And it came to pass, that when Jeremiah had made an end of speaking unto all the people all the words of the LORD their God, wherewith the LORD their God had sent him to them, even all these words,
Yeremiya atatsiriza kuwawuza anthuwo mawu onse a Yehova Mulungu wawo, amene Yehova anamutuma kuti akawawuze,
2 then spoke Azariah the son of Hoshaiah, and Johanan the son of Kareah, and all the proud men, saying unto Jeremiah: 'Thou speakest falsely; the LORD our God hath not sent thee to say: Ye shall not go into Egypt to sojourn there;
Azariya mwana wa Hosayia ndi Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi anthu onse odzikuza anawuza Yeremiya kuti, “Ukunama iwe! Yehova Mulungu wathu sanakutume kuti unene kuti, ‘Musapite ku Igupto kukakhala kumeneko.’
3 but Baruch the son of Neriah setteth thee on against us, to deliver us into the hand of the Chaldeans, that they may put us to death, and carry us away captives to Babylon.'
Koma ndi Baruki mwana wa Neriya amene akukulimbikitsa kuti utiletse zopita ku Igupto ndi kuti mʼmalo mwake tidzipereke mʼmanja mwa Ababuloni, kuti iwo atiphe kapena kutitenga ukapolo ku Babuloni.”
4 So Johanan the son of Kareah, and all the captains of the forces, and all the people, hearkened not to the voice of the LORD, to dwell in the land of Judah.
Motero Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi anthu onse sanamvere lamulo la Yehova loti akhale mʼdziko la Yuda.
5 But Johanan the son of Kareah, and all the captains of the forces, took all the remnant of Judah, that were returned from all the nations whither they had been driven to sojourn in the land of Judah:
Mʼmalo mwake, Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo anatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene anabwera kudzakhala mʼdziko la Yuda kuchokera ku mayiko onse kumene anabalakirako.
6 the men, and the women, and the children, and the king's daughters, and every person that Nebuzaradan the captain of the guard had left with Gedaliah the son of Ahikam, the son of Shaphan, and Jeremiah the prophet, and Baruch the son of Neriah;
Mʼgulu la anthu otengedwalo munali amuna onse, akazi ndi ana, ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anawasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani pamodzinso ndi mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya.
7 and they came into the land of Egypt; for they hearkened not to the voice of the LORD; and they came even to Tahpanhes.
Kotero anthuwo analowa mʼdziko la Igupto chifukwa anakana kumvera Yehova, nakafika ku Tapanesi.
8 Then came the word of the LORD unto Jeremiah in Tahpanhes, saying:
Ndipo Yehova anayankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi kuti,
9 'Take great stones in thy hand, and hide them in the mortar in the framework, which is at the entry of Pharaoh's house in Tahpanhes, in the sight of the men of Judah;
“Tenga miyala inayi yayikulu ndipo uyikwirire mʼdothi pa chiwundo cha polowera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Uchite zimenezi Ayuda onse akuona.
10 and say unto them: Thus saith the LORD of hosts, the God of Israel: Behold, I will send and take Nebuchadrezzar the king of Babylon, My servant, and will set his throne upon these stones that I have hid; and he shall spread his royal pavilion over them.
Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayitana mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzakhazika mpando wake waufumu pa miyala imene ndayikwirira apayi. Iye adzafunyulula tenti yake yaufumu pa miyala imeneyi.
11 And he shall come, and shall smite the land of Egypt; such as are for death to death, and such as are for captivity to captivity, and such as are for the sword to the sword.
Iye adzabwera kudzathira nkhondo Igupto. Iwo oyenera kufa ndi mliri adzafa ndi mliri, iwo oyenera kutengedwa ukapolo adzatengedwa ukapolo, ndipo iwo oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
12 And I will kindle a fire in the houses of the gods of Egypt; and he shall burn them, and carry them away captives; and he shall fold up the land of Egypt, as a shepherd foldeth up his garment; and he shall go forth from thence in peace.
Adzayatsa moto mʼnyumba zopembedzera milungu ya Igupto. Adzayeretsa dziko la Igupto monga momwe mʼbusa amayeretsera chovala chake pochotsamo nsabwe. Pambuyo pake adzachoka mʼdziko la Igupto mwa mtendere.
13 He shall also break the pillars of Beth-shemesh, that is in the land of Egypt; and the houses of the gods of Egypt shall he burn with fire.'
Ku Iguptoko adzagwetsa zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzera mulungu wa dzuwa. Adzatentha ndi moto nyumba za milungu ya ku Igupto.’”

< Jeremiah 43 >