< Isaiah 62 >

1 For Zion's sake will I not hold My peace, and for Jerusalem's sake I will not rest, until her triumph go forth as brightness, and her salvation as a torch that burneth.
Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete, chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete, mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala, ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.
2 And the nations shall see thy triumph, and all kings thy glory; and thou shalt be called by a new name, which the mouth of the LORD shall mark out.
Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako. Adzakuyitanira dzina latsopano limene adzakupatse ndi Yehova.
3 Thou shalt also be a crown of beauty in the hand of the LORD, and a royal diadem in the open hand of thy God.
Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova, ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.
4 Thou shalt no more be termed Forsaken, neither shall thy land any more be termed Desolate; but thou shalt be called, My delight is in her, and thy land, Espoused; for the LORD delighteth in thee, and thy land shall be espoused.
Sadzakutchanso “Wosiyidwa,” ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.” Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.” Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.” Chifukwa Yehova akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
5 For as a young man espouseth a virgin, so shall thy sons espouse thee; and as the bridegroom rejoiceth over the bride, so shall thy God rejoice over thee.
Monga mnyamata amakwatira namwali, momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira; monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi, chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.
6 I have set watchmen upon thy walls, O Jerusalem, they shall never hold their peace day nor night: 'Ye that are the LORD'S remembrancers, take ye no rest,
Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda; sadzakhala chete usana kapena usiku. Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake musapumule.
7 And give Him no rest, till He establish, and till He make Jerusalem a praise in the earth.'
Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.
8 The LORD hath sworn by His right hand, and by the arm of His strength: Surely I will no more give thy corn to be food for thine enemies; and strangers shall not drink thy wine, for which thou hast laboured;
Yehova analumbira atakweza dzanja lake. Anati, “Sindidzaperekanso tirigu wako kuti akhale chakudya cha adani ako, ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano pakuti unamuvutikira.
9 But they that have garnered it shall eat it, and praise the LORD, and they that have gathered it shall drink it in the courts of My sanctuary.
Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi ndi kutamanda Yehova, ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo mʼmabwalo a Nyumba yanga.”
10 Go through, go through the gates, clear ye the way of the people; cast up, cast up the highway, gather out the stones; lift up an ensign over the peoples.
Tulukani, dutsani pa zipata! Konzerani anthu njira. Lambulani, lambulani msewu waukulu! Chotsani miyala. Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.
11 Behold, the LORD hath proclaimed unto the end of the earth: say ye to the daughter of Zion: 'Behold, thy salvation cometh; behold, His reward is with Him, and His recompense before Him.'
Yehova walengeza ku dziko lonse lapansi kuti, Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti, “Taonani, chipulumutso chanu chikubwera; Yehova akubwera ndi mphotho yake akubwera nazo zokuyenerani.”
12 And they shall call them The holy people, The redeemed of the LORD; and thou shalt be called Sought out, a city not forsaken.
Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika, owomboledwa a Yehova; ndipo adzakutchani “Okondwa a Yehova” “Mzinda umene Yehova sanawusiye.”

< Isaiah 62 >