< Isaiah 56 >

1 Thus saith the LORD: Keep ye justice, and do righteousness; for My salvation is near to come, and My favour to be revealed.
Yehova akuti, “Chitani chilungamo ndi zinthu zabwino, chifukwa chipulumutso changa chili pafupi ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
2 Happy is the man that doeth this, and the son of man that holdeth fast by it: that keepeth the sabbath from profaning it, and keepeth his hand from doing any evil.
Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi, munthu amene amalimbika kuzichita, amene amasunga Sabata osaliyipitsa, ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
3 Neither let the alien, that hath joined himself to the LORD, speak, saying: 'The LORD will surely separate me from His people'; neither let the eunuch say: 'Behold, I am a dry tree.'
Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti, “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.” Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti, “Ine ndine mtengo wowuma basi.”
4 For thus saith the LORD concerning the eunuchs that keep My sabbaths, and choose the things that please Me, and hold fast by My covenant:
Popeza Yehova akuti, “Wofulidwa amene amasunga masabata anga, nachita zokomera Ine ndi kusunga pangano langa,
5 Even unto them will I give in My house and within My walls a monument and a memorial better than sons and daughters; I will give them an everlasting memorial, that shall not be cut off.
ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake, kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi. Ndidzawapatsa dzina labwino, losatha ndi losayiwalika.”
6 Also the aliens, that join themselves to the LORD, to minister unto Him, and to love the name of the LORD, to be His servants, every one that keepeth the sabbath from profaning it, and holdeth fast by My covenant:
Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova, motero kuti amamutumikira Iye, amakonda dzina la Yehova, amamugwirira ntchito, komanso kusunga Sabata osaliyipitsa ndi kusunga bwino pangano langa,
7 Even them will I bring to My holy mountain, and make them joyful in My house of prayer; their burnt-offerings and their sacrifices shall be acceptable upon Mine altar; for My house shall be called a house of prayer for all peoples.
amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika, ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero. Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe. Paja nyumba yanga idzatchedwa nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
8 Saith the Lord GOD who gathereth the dispersed of Israel: Yet I will gather others to him, beside those of him that are gathered.
Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti, “Ndidzasonkhanitsano anthu ena kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
9 All ye beasts of the field, come to devour, yea, all ye beasts in the forest.
Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo, inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
10 His watchmen are all blind, without knowledge; they are all dumb dogs, they cannot bark; raving, lying down, loving to slumber.
Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu, onse ndi opanda nzeru; onse ndi agalu opanda mawu, samatha kuwuwa: amagona pansi nʼkumalota amakonda kugona tulo.
11 Yea, the dogs are greedy, they know not when they have enough; and these are shepherds that cannot understand; they all turn to their own way, each one to his gain, one and all.
Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu; sakhuta konse. Abusa nawonso samvetsa zinthu; onse amachita monga akufunira, aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
12 'Come ye, I will fetch wine, and we will fill ourselves with strong drink; and to-morrow shall be as this day, and much more abundant.'
Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo! Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta! Mawa lidzakhala ngati leroli, kapena kuposa lero lino.”

< Isaiah 56 >