< Isaiah 50 >

1 Thus saith the LORD: Where is the bill of your mother's divorcement, wherewith I have put her away? Or which of My creditors is it to whom I have sold you? Behold, for your iniquities were ye sold, and for your transgressions was your mother put away.
Yehova akuti, “Kalata imene ndinasudzulira amayi anu ili kuti? Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole, ndinakugulitsani kwa ati? Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu; amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.
2 Wherefore, when I came, was there no man? when I called, was there none to answer? Is My hand shortened at all, that it cannot redeem? Or have I no power to deliver? Behold, at My rebuke I dry up the sea, I make the rivers a wilderness; their fish become foul, because there is no water, and die for thirst.
Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu? Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha? Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani? Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani? Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu, mitsinje ndinayisandutsa chipululu; nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi; ndipo zinafa ndi ludzu.
3 I clothe the heavens with blackness, and I make sackcloth their covering.
Ndinaphimba thambo ndi mdima ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”
4 The Lord GOD hath given me the tongue of them that are taught, that I should know how to sustain with words him that is weary; He wakeneth morning by morning, He wakeneth mine ear to hear as they that are taught.
Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka. Mmawa mulimonse amandidzutsa, amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.
5 The Lord GOD hath opened mine ear, and I was not rebellious, neither turned away backward.
Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga, ndipo sindinakhale munthu wowukira ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.
6 I gave my back to the smiters, and my checks to them that plucked off the hair; I hid not my face from shame and spitting.
Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu; sindinawabisire nkhope yanga anthu ondinyoza ndi ondilavulira.
7 For the Lord GOD will help me; therefore have I not been confounded; therefore have I set my face like a flint, and I know that I shall not be ashamed.
Popeza Ambuye Yehova amandithandiza, sindidzachita manyazi. Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi, chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.
8 He is near that justifieth me; who will contend with me? let us stand up together; who is mine adversary? let him come near to me.
Wondikhalira kumbuyo ali pafupi, ndaninso amene adzandiyimba mlandu? Abwere kuti tionane maso ndi maso! Mdani wanga ndi ndani? Abweretu kuti tilimbane!
9 Behold, the Lord GOD will help me; who is he that shall condemn me? Behold, they all shall wax old as a garment, the moth shall eat them up.
Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza. Ndaninso amene adzanditsutsa? Onse adzatha ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
10 Who is among you that feareth the LORD, that obeyeth the voice of His servant? though he walketh in darkness, and hath no light, let him trust in the name of the LORD, and stay upon his God.
Ndani mwa inu amaopa Yehova ndi kumvera mawu a mtumiki wake? Aliyense woyenda mu mdima, popanda chomuwunikira, iye akhulupirire dzina la Yehova ndi kudalira Mulungu wake.
11 Behold, all ye that kindle a fire, that gird yourselves with firebrands, begone in the flame of your fire, and among the brands that ye have kindled. This shall ye have of My hand; ye shall lie down in sorrow.
Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu, lowani mʼmoto wanu womwewo. Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa. Ndipo ine Yehova ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.

< Isaiah 50 >