< Isaiah 43 >

1 But now thus saith the LORD that created thee, O Jacob, and He that formed thee, O Israel: Fear not, for I have redeemed thee, I have called thee by thy name, thou art Mine.
Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
2 When thou passest through the waters, I will be with thee, and through the rivers, they shall not overflow thee; when thou walkest through the fire, thou shalt not be burned, neither shall the flame kindle upon thee.
Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
3 For I am the LORD thy God, The Holy One of Israel, thy Saviour; I have given Egypt as thy ransom, Ethiopia and Seba for thee.
Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
4 Since thou art precious in My sight, and honourable, and I have loved thee; therefore will I give men for thee, and peoples for thy life.
Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
5 Fear not, for I am with thee; I will bring thy seed from the east, and gather thee from the west;
Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
6 I will say to the north: 'Give up,' and to the south: 'Keep not back, bring My sons from far, and My daughters from the end of the earth;
Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
7 Every one that is called by My name, and whom I have created for My glory, I have formed him, yea, I have made him.'
onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
8 The blind people that have eyes shall be brought forth, and the deaf that have ears.
Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
9 All the nations are gathered together, and the peoples are assembled; who among them can declare this, and announce to us former things? Let them bring their witnesses, that they may be justified; and let them hear, and say: 'It is truth.'
Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
10 Ye are My witnesses, saith the LORD, and My servant whom I have chosen; that ye may know and believe Me, and understand that I am He; before Me there was no God formed, neither shall any be after Me.
Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
11 I, even I, am the LORD; and beside Me there is no saviour.
Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
12 I have declared, and I have saved, and I have announced, and there was no strange god among you; therefore ye are My witnesses, saith the LORD, and I am God.
Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
13 Yea, since the day was I am He, and there is none that can deliver out of My hand; I will work, and who can reverse it?
“Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
14 Thus saith the LORD, your Redeemer, The Holy One of Israel: For your sake I have sent to Babylon, and I will bring down all of them as fugitives, even the Chaldeans, in the ships of their shouting.
Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
15 I am the LORD, your Holy One, the Creator of Israel, your King.
Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
16 Thus saith the LORD, who maketh a way in the sea, and a path in the mighty waters;
Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
17 Who bringeth forth the chariot and horse, the army and the power — they lie down together, they shall not rise, they are extinct, they are quenched as a wick:
Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
18 Remember ye not the former things, neither consider the things of old.
“Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
19 Behold, I will do a new thing; now shall it spring forth; shall ye not know it? I will even make a way in the wilderness, and rivers in the desert.
Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
20 The beasts of the field shall honour Me, the jackals and the ostriches; because I give waters in the wilderness, and rivers in the desert, to give drink to My people, Mine elect;
Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
21 The people which I formed for Myself, that they might tell of My praise.
Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
22 Yet thou hast not called upon Me, O Jacob, neither hast thou wearied thyself about Me, O Israel.
“Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
23 Thou hast not brought Me the small cattle of thy burnt-offerings; neither hast thou honoured Me with thy sacrifices. I have not burdened thee with a meal-offering, nor wearied thee with frankincense.
Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
24 Thou hast bought Me no sweet cane with money, neither hast thou satisfied Me with the fat of thy sacrifices; but thou hast burdened Me with thy sins, thou hast wearied Me with thine iniquities.
Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
25 I, even I, am He that blotteth out thy transgressions for Mine own sake; and thy sins I will not remember.
“Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
26 Put Me in remembrance, let us plead together; declare thou, that thou mayest be justified.
Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
27 Thy first father sinned, and thine intercessors have transgressed against Me.
Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
28 Therefore I have profaned the princes of the sanctuary, and I have given Jacob to condemnation, and Israel to reviling.
Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”

< Isaiah 43 >