< Isaiah 29 >

1 Ah, Ariel, Ariel, the city where David encamped! Add ye year to year, let the feasts come round!
Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli, mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo! Papite chaka chimodzi kapena ziwiri ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
2 Then will I distress Ariel, and there shall be mourning and moaning; and she shall be unto Me as a hearth of God.
Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula, mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
3 And I will encamp against thee round about, and will lay siege against thee with a mound, and I will raise siege works against thee.
Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo; ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
4 And brought down thou shalt speak out of the ground, and thy speech shall be low out of the dust; and thy voice shall be as of a ghost out of the ground, and thy speech shall chirp out of the dust.
Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka, mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi, adzamveka ngati a mzukwa. Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.
5 But the multitude of thy foes shall be like small dust, and the multitude of the terrible ones as chaff that passeth away; yea, it shall be at an instant suddenly —
Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti. Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo. Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
6 There shall be a visitation from the LORD of hosts with thunder, and with earthquake, and great noise, with whirlwind and tempest, and the flame of a devouring fire.
Yehova Wamphamvuzonse adzabwera ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu, kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
7 And the multitude of all the nations that war against Ariel, even all that war against her, and the bulwarks about her, and they that distress her, shall be as a dream, a vision of the night.
Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga, chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto, gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
8 And it shall be as when a hungry man dreameth, and, behold, he eateth, but he awaketh, and his soul is empty; or as when a thirsty man dreameth, and, behold, he drinketh, but he awaketh, and, behold, he is faint, and his soul hath appetite — so shall the multitude of all the nations be, that fight against mount Zion.
Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya, koma podzuka ali nayobe njala; kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa, koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa. Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.
9 Stupefy yourselves, and be stupid! Blind yourselves, and be blind! ye that are drunken, but not with wine, that stagger, but not with strong drink.
Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa. Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya, ledzerani, koma osati ndi vinyo, dzandirani, koma osati ndi mowa.
10 For the LORD hath poured out upon you the spirit of deep sleep, and hath closed your eyes; the prophets, and your heads, the seers, hath He covered.
Yehova wakugonetsani tulo tofa nato. Watseka maso anu, inu aneneri; waphimba mitu yanu, inu alosi.
11 And the vision of all this is become unto you as the words of a writing that is sealed, which men deliver to one that is learned, saying: 'Read this, I pray thee'; and he saith: 'I cannot, for it is sealed';
Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.”
12 and the writing is delivered to him that is not learned, saying: 'Read this, I pray thee'; and he saith: 'I am not learned.'
Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”
13 And the Lord said: Forasmuch as this people draw near, and with their mouth and with their lips do honour Me, but have removed their heart far from Me, and their fear of Me is a commandment of men learned by rote;
Ambuye akuti, “Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo, ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine. Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso. Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
14 Therefore, behold, I will again do a marvellous work among this people, even a marvellous work and a wonder; and the wisdom of their wise men shall perish, and the prudence of their prudent men shall be hid.
Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira kuwachitira ntchito zodabwitsa; nzeru za anthu anzeru zidzatha, luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
15 Woe unto them that seek deep to hide their counsel from the LORD, and their works are in the dark, and they say: 'Who seeth us? and who knoweth us?'
Tsoka kwa amene amayesetsa kubisira Yehova maganizo awo, amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti, “Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
16 O your perversity! Shall the potter be esteemed as clay; that the thing made should say of him that made it: 'He made me not'; or the thing framed say of him that framed it: 'He hath no understanding?'
Inu mumazondotsa zinthu ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya. Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti “Sunandipange ndi iwe?” Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti, “Iwe sudziwa chilichonse?”
17 Is it not yet a very little while, and Lebanon shall be turned into a fruitful field, and the fruitful field shall be esteemed as a forest?
Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde, ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
18 And in that day shall the deaf hear the words of a book, and the eyes of the blind shall see out of obscurity and out of darkness.
Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku, ndipo anthu osaona amene ankakhala mu mdima adzapenya.
19 The humble also shall increase their joy in the LORD, and the neediest among men shall exult in the Holy One of Israel.
Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova; ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
20 For the terrible one is brought to nought, and the scorner ceaseth, and all they that watch for iniquity are cut off;
Koma anthu ankhanza adzazimirira, oseka anzawo sadzaonekanso, ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
21 That make a man an offender by words, and lay a snare for him that reproveth in the gate, and turn aside the just with a thing of nought.
Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa, kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.
22 Therefore thus saith the LORD, who redeemed Abraham, concerning the house of Jacob: Jacob shall not now be ashamed, neither shall his face now wax pale;
Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti, “Anthu anga sadzachitanso manyazi; nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
23 When he seeth his children, the work of My hands, in the midst of him, that they sanctify My name; yea, they shall sanctify the Holy One of Jacob, and shall stand in awe of the God of Israel.
Akadzaona ana awo ndi ntchito ya manja anga pakati pawo, adzatamanda dzina langa loyera; adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo, ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
24 They also that err in spirit shall come to understanding, and they that murmur shall learn instruction.
Anthu opusa adzapeza nzeru; onyinyirika adzalandira malangizo.”

< Isaiah 29 >