< Isaiah 22 >

1 The burden concerning the Valley of Vision. What aileth thee now, that thou art wholly gone up to the housetops,
Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
2 Thou that art full of uproar, a tumultuous city, a joyous town? Thy slain are not slain with the sword, nor dead in battle.
Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
3 All thy rulers are fled together, without the bow they are bound; all that are found of thee are bound together, they are fled afar off.
Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
4 Therefore said I: 'Look away from me, I will weep bitterly; strain not to comfort me, for the destruction of the daughter of my people.'
Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
5 For it is a day of trouble, and of trampling, and of perplexity, from the Lord, the GOD of hosts, in the Valley of Vision; Kir shouting, and Shoa at the mount.
Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
6 And Elam bore the quiver, with troops of men, even horsemen; and Kir uncovered the shield.
Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
7 And it came to pass, when thy choicest valleys were full of chariots, and the horsemen set themselves in array at the gate,
Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
8 And the covering of Judah was laid bare, that thou didst look in that day to the armour in the house of the forest.
zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
9 And ye saw the breaches of the city of David, that they were many; and ye gathered together the waters of the lower pool.
inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
10 And ye numbered the houses of Jerusalem, and ye broke down the houses to fortify the wall;
Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
11 ye made also a basin between the two walls for the water of the old pool — but ye looked not unto Him that had done this, neither had ye respect unto Him that fashioned it long ago.
Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
12 And in that day did the Lord, the GOD of hosts, call to weeping, and to lamentation, and to baldness, and to girding with sackcloth;
Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
13 And behold joy and gladness, slaying oxen and killing sheep, eating flesh and drinking wine — 'Let us eat and drink, for tomorrow we shall die!'
Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
14 And the LORD of hosts revealed Himself in mine ears: Surely this iniquity shall not be expiated by you till ye die, saith the Lord, the GOD of hosts.
Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
15 Thus saith the Lord, the GOD of hosts: Go, get thee unto this steward, even unto Shebna, who is over the house:
Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
16 What hast thou here, and whom hast thou here, that thou hast hewed thee out here a sepulchre, thou that hewest thee out a sepulchre on high, and gravest a habitation for thyself in the rock?
Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
17 Behold, the LORD will hurl thee up and down with a man's throw; yea, He will wind thee round and round;
“Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
18 He will violently roll and toss thee like a ball into a large country; there shalt thou die, and there shall be the chariots of thy glory, thou shame of the lord's house.
Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
19 And I will thrust thee from thy post, and from thy station shalt thou be pulled down.
Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
20 And it shall come to pass in that day, that I will call my servant Eliakim the son of Hilkiah;
“Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
21 And I will clothe him with thy robe, and bind him with thy girdle, and I will commit thy government into his hand; and he shall be a father to the inhabitants of Jerusalem, and to the house of Judah.
Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
22 And the key of the house of David will I lay upon his shoulder; and he shall open, and none shall shut; and he shall shut, and none shall open.
Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
23 And I will fasten him as a peg in a sure place; and he shall be for a throne of honour to his father's house.
Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
24 And they shall hang upon him all the glory of his father's house, the offspring and the issue, all vessels of small quantity, from the vessels of cups even to all the vessels of flagons.
Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
25 In that day, saith the LORD of hosts, shall the peg that was fastened in a sure place give way; and it shall be hewn down, and fall, and the burden that was upon it shall be cut off; for the LORD hath spoken it.
“Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.

< Isaiah 22 >