< Hosea 7 >
1 when I would heal Israel, then is the iniquity of Ephraim uncovered, and the wickedness of Samaria, for they commit falsehood; and the thief entereth in, and the troop of robbers maketh a raid without.
Pamene ndichiritsa Israeli, machimo a Efereimu amaonekera poyera ndiponso milandu ya Samariya sibisika. Iwo amachita zachinyengo, mbala zimathyola nyumba, achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.
2 And let them not say to their heart — I remember all their wickedness; now their own doings have beset them about, they are before My face.
Koma sazindikira kuti Ine ndimakumbukira zoyipa zawo zonse. Azunguliridwa ndi zolakwa zawo; ndipo sizichoka mʼmaso mwanga.
3 They make the king glad with their wickedness, and the princes with their lies.
“Anthuwa amasangalatsa mfumu ndi zoyipa zawozo, akalonga amasekerera mabodza awo.
4 They are all adulterers, as an oven heated by the baker, who ceaseth to stir from the kneading of the dough until it be leavened.
Onsewa ndi anthu azigololo, otentha ngati moto wa mu uvuni, umene wophika buledi sasonkhezera kuyambira pamene akukanda buledi mpaka atafufuma.
5 On the day of our king the princes make him sick with the heat of wine, he stretcheth out his hand with scorners.
Pa tsiku la chikondwerero cha mfumu yathu akalonga amaledzera ndi vinyo, ndipo amalowa mʼgulu la anthu achipongwe.
6 For they have made ready their heart like an oven, while they lie in wait; their baker sleepeth all the night, in the morning it burneth as a flaming fire.
Mitima yawo ili ngati uvuni; amayandikira Mulungu mwachiwembu. Ukali wawo umanyeka usiku wonse, mmawa umayaka ngati malawi a moto.
7 They are all hot as an oven, and devour their judges; all their kings are fallen, there is none among them that calleth unto Me.
Onsewa ndi otentha ngati uvuni, amapha olamulira awo. Mafumu awo onse amagwa, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amandiyitana Ine.
8 Ephraim, he mixeth himself with the peoples; Ephraim is become a cake not turned.
“Efereimu wasakanikirana ndi mitundu ya anthu ena; Efereimu ndi buledi amene wapsa mbali imodzi.
9 Strangers have devoured his strength, and he knoweth it not; yea, gray hairs are here and there upon him, and he knoweth it not.
Alendo atha mphamvu zake, koma iye sakuzindikira. Tsitsi lake layamba imvi koma iye sakudziwa.
10 And the pride of Israel testifieth to his face; but they have not returned unto the LORD their God, nor sought Him, for all this.
Kunyada kwake Israeli kukumutsutsa, koma pa zonsezi iye sakubwerera kwa Yehova Mulungu wake kapena kumufunafuna.
11 And Ephraim is become like a silly dove, without understanding; they call unto Egypt, they go to Assyria.
“Efereimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru. Amayitana Igupto namapita ku Asiriya.
12 Even as they go, I will spread My net upon them; I will bring them down as the fowls of the heaven; I will chastise them, as their congregation hath been made to hear.
Akamadzapita, ndidzawakola ndi ukonde wanga; ndidzawagwetsa pansi ngati mbalame zamumlengalenga. Ndikadzamva kuti asonkhana pamodzi ndidzawakola.
13 Woe unto them! for they have strayed from Me; Destruction unto them! for they have transgressed against Me; Shall I then redeem them, seeing they have spoken lies against Me?
Tsoka kwa iwo, chifukwa andisiya Ine! Chiwonongeko kwa iwo, chifukwa andiwukira! Ndimafunitsitsa kuwapulumutsa koma amayankhula za Ine monama.
14 And they have not cried unto Me with their heart, though they wail upon their beds; they assemble themselves for corn and wine, they rebel against Me.
Iwo salirira kwa Ine kuchokera pansi pa mtima, koma amalira mofuwula ali pa bedi pawo. Amadzichekacheka chifukwa chofuna tirigu ndi vinyo watsopano, koma amandifulatira.
15 Though I have trained and strengthened their arms, yet do they devise evil against Me.
Ine ndinawaphunzitsa ndikuwalimbitsa, koma amandikonzera chiwembu.
16 They return, but not upwards; they are become like a deceitful bow; their princes shall fall by the sword for the rage of their tongue; this shall be their derision in the land of Egypt.
Iwo satembenukira kwa Wammwambamwamba; ali ngati uta woonongeka. Atsogoleri awo adzaphedwa ndi lupanga chifukwa cha mawu awo achipongwe. Motero iwo adzasekedwa mʼdziko la Igupto.