< Hosea 5 >

1 Hear this, O ye priests, and attend, ye house of Israel, and give ear, O house of the king, for unto you pertaineth the judgment; for ye have been a snare on Mizpah, and a net spread upon Tabor.
“Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
2 And they that fall away are gone deep in making slaughter; and I am rejected of them all.
Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
3 I, even I, know Ephraim, and Israel is not hid from Me; for now, O Ephraim, thou hast committed harlotry, Israel is defiled.
Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
4 Their doings will not suffer them to return unto their God; for the spirit of harlotry is within them, and they know not the LORD.
“Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
5 But the pride of Israel shall testify to his face; and Israel and Ephraim shall stumble in their iniquity, Judah also shall stumble with them.
Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
6 With their flocks and with their herds they shall go to seek the LORD, but they shall not find Him; He hath withdrawn Himself from them.
Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
7 They have dealt treacherously against the LORD, for they have begotten strange children; now shall the new moon devour them with their portions.
Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
8 Blow ye the horn in Gibeah, and the trumpet in Ramah; sound an alarm at Beth-aven: 'Behind thee, O Benjamin!'
“Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
9 Ephraim shall be desolate in the day of rebuke; among the tribes of Israel do I make known that which shall surely be.
Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
10 The princes of Judah are like them that remove the landmark; I will pour out My wrath upon them like water.
Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
11 Oppressed is Ephraim, crushed in his right; because he willingly walked after filth.
Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
12 Therefore am I unto Ephraim as a moth, and to the house of Judah as rottenness.
Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
13 And when Ephraim saw his sickness, and Judah his wound, Ephraim went to Assyria, and sent to King Contentious; but he is not able to heal you, neither shall he cure you of your wound.
“Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
14 For I will be unto Ephraim as a lion, and as a young lion to the house of Judah; I, even I, will tear and go away, I will take away, and there shall be none to deliver.
Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
15 I will go and return to My place, till they acknowledge their guilt, and seek My face; in their trouble they will seek Me earnestly:
Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”

< Hosea 5 >