< Genesis 20 >

1 And Abraham journeyed from thence toward the land of the South, and dwelt between Kadesh and Shur; and he sojourned in Gerar.
Abrahamu anachokako kumeneko napita ku Negevi ndipo anakakhala ku dziko la Gerari, limene lili pakati pa mzinda wa Kadesi ndi mzinda wa Suri. Anakhala ku Gerari kwa kanthawi,
2 And Abraham said of Sarah his wife: 'She is my sister.' And Abimelech king of Gerar sent, and took Sarah.
ndipo Abrahamu ankawawuza za Sara kuti, “Iyeyu ndi mlongo wanga.” Choncho Abimeleki, mfumu wa ku Gerari anamutenga Sara uja.
3 But God came to Abimelech in a dream of the night, and said to him: 'Behold, thou shalt die, because of the woman whom thou hast taken; for she is a man's wife.'
Koma usiku, Mulungu anafika kwa Abimeleki kutulo nati, “Ufatu iwe chifukwa cha mkazi amene watengayu popeza ndi wokwatiwa.”
4 Now Abimelech had not come near her; and he said: 'Lord, wilt Thou slay even a righteous nation?
Nthawi imeneyi nʼkuti Abimeleki asanamukhudze mkaziyo, kotero kuti anati, “Ambuye, kodi mudzawonongadi mtundu wolungama?
5 Said he not himself unto me: She is my sister? and she, even she herself said: He is my brother. In the simplicity of my heart and the innocency of my hands have I done this.'
Kodi Abrahamu sanandiwuze kuti iyeyu ndi mlongo wake? Ndiponso mkaziyu ankanena kuti Abrahamu ndi mlongo wake. Choncho ine pochita izi, ndinkachita moona mtima ndiponso mopanda chinyengo.”
6 And God said unto him in the dream: 'Yea, I know that in the simplicity of thy heart thou hast done this, and I also withheld thee from sinning against Me. Therefore suffered I thee not to touch her.
Tsono kumaloto komweko Mulungu anati kwa iye, “Inde ndikudziwa kuti wachita izi moona mtima, ndipo Ine sindinafune kuti undichimwire. Nʼchifukwa chake sindinakulole kuti umukhudze.
7 Now therefore restore the man's wife; for he is a prophet, and he shall pray for thee, and thou shalt live; and if thou restore her not, know thou that thou shalt surely die, thou, and all that are thine.'
Tsopano kabwezere mkaziyo kwa mwamuna wake. Iyeyu ndi mneneri, ndipo adzakupempherera kuti ukhale ndi moyo. Koma ukapanda kukamupereka, udziwiretu kuti udzafa pamodzi ndi onse a pa banja pako.”
8 And Abimelech rose early in the morning, and called all his servants, and told all these things in their ears; and the men were sore afraid.
Mmamawa mwake Abimeleki anayitanitsa akuluakulu ake onse, ndipo atawafotokozera zimene zinachitika, iwo aja anachita mantha kwambiri.
9 Then Abimelech called Abraham, and said unto him: 'What hast thou done unto us? and wherein have I sinned against thee, that thou hast brought on me and on my kingdom a great sin? thou hast done deeds unto me that ought not to be done.'
Kenaka Abimeleki anayitana Abrahamu ndipo anati, “Kodi wachita chiyani? Ndakulakwira chiyani kuti undibweretsere ine pamodzi ndi anthu anga chilango chachikulu chotere? Wandichitira zinthu zimene sizinayenera kuchitika.”
10 And Abimelech said unto Abraham: 'What sawest thou, that thou hast done this thing?'
Ndipo Abrahamu anafunsa Abimeleki kuti, “Chifukwa chiyani wachita zimenezi?”
11 And Abraham said: 'Because I thought: Surely the fear of God is not in this place; and they will slay me for my wife's sake.
Abrahamu anayankha nati, “Ndinkaganiza kuti kuno kulibiretu munthu woopa Mulungu. Ndiye ndimati mwina adzandipha chifukwa cha mkazi wanga.
12 And moreover she is indeed my sister, the daughter of my father, but not the daughter of my mother; and so she became my wife.
Komabe kunena zoona, iyeyu ndi mlongo wangadi, mwana wamkazi wa abambo anga ngakhale kuti si ife a mayi mmodzi. Tsono akhoza kukhala mkazi wanga.
13 And it came to pass, when God caused me to wander from my father's house, that I said unto her: This is thy kindness which thou shalt show unto me; at every place whither we shall come, say of me: He is my brother.'
Ndiye pamene Mulungu anati ndichoke ku nyumba ya abambo anga, ndinawuza mkazi wangayu kuti, ‘Kuti uwonetse kuti ndiwe mkazi wokoma mtima, uziwuza anthu kulikonse kumene tingapite kuti ndine mlongo wako.’”
14 And Abimelech took sheep and oxen, and men-servants and women-servants, and gave them unto Abraham, and restored him Sarah his wife.
Tsono Abimeleki anapereka nkhosa, ngʼombe ndi antchito aamuna ndi aakazi kwa Abrahamu. Ndipo anamubwezeranso Abrahamu Sara, mkazi wake.
15 And Abimelech said: 'Behold, my land is before thee: dwell where it pleaseth thee.'
Tsono Abimeleki anati kwa Abrahamu, “Dziko langa ndi limene ukulionali; ukhale paliponse pamene ufuna.”
16 And unto Sarah he said: 'Behold, I have given thy brother a thousand pieces of silver; behold, it is for thee a covering of the eyes to all that are with thee; and before all men thou art righted.'
Ndipo kwa Sara, iye anati, “Ndikumupatsa mlongo wakoyu makilogalamu khumi ndi awiri a siliva kutsimikiza kuti iwe ndi wosalakwa pamaso pa onse amene ali ndi iwe; ulibedi mlandu.”
17 And Abraham prayed unto God; and God healed Abimelech, and his wife, and his maid-servants; and they bore children.
Tsono Abrahamu anapemphera kwa Mulungu ndipo Mulunguyo anachiritsa Abimeleki, mkazi wake pamodzi ndi adzakazi ake kuti athenso kubereka ana.
18 For the LORD had fast closed up all the wombs of the house of Abimelech, because of Sarah Abraham's wife.
Paja Yehova nʼkuti atatseka akazi onse a mʼbanja la Abimeleki kuti asabereke ana chifukwa cha Sara, mkazi wa Abrahamu.

< Genesis 20 >