< Ezekiel 39 >
1 And thou, son of man, prophesy against Gog, and say: Thus saith the Lord GOD: Behold, I am against thee, O Gog, chief prince of Meshech and Tubal;
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 and I will turn thee about and lead thee on, and will cause thee to come up from the uttermost parts of the north; and I will bring thee upon the mountains of Israel;
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 and I will smite thy bow out of thy left hand, and will cause thine arrows to fall out of thy right hand.
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 Thou shalt fall upon the mountains of Israel, thou, and all thy bands, and the peoples that are with thee; I will give thee unto the ravenous birds of every sort and to the beasts of the field, to be devoured.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 Thou shalt fall upon the open field; for I have spoken it, saith the Lord GOD.
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 And I will send a fire on Magog, and on them that dwell safely in the isles; and they shall know that I am the LORD.
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 And My holy name will I make known in the midst of My people Israel; neither will I suffer My holy name to be profaned any more; and the nations shall know that I am the LORD, the Holy One in Israel.
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 Behold, it cometh, and it shall be done, saith the Lord GOD; This is the day whereof I have spoken.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 And they that dwell in the cities of Israel shall go forth, and shall make fires of the weapons and use them as fuel, both the shields and the bucklers, the bows and the arrows, and the hand-staves, and the spears, and they shall make fires of them seven years;
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 so that they shall take no wood out of the field, neither cut down any out of the forests, for they shall make fires of the weapons; and they shall spoil those that spoiled them, and rob those that robbed them, saith the Lord GOD.
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 And it shall come to pass in that day, that I will give unto Gog a place fit for burial in Israel, the valley of them that pass through on the east of the sea; and it shall stop them that pass through; and there shall they bury Gog and all his multitude; and they shall call it the valley of Hamon-gog.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 And seven months shall the house of Israel be burying them, that they may cleanse the land.
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 Yea, all the people of the land shall bury them, and it shall be to them a renown; in the day that I shall be glorified, saith the Lord GOD.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 And they shall set apart men of continual employment, that shall pass through the land to bury with them that pass through those that remain upon the face of the land, to cleanse it; after the end of seven months shall they search.
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 And when they that pass through shall pass through the land, and any seeth a man's bone, then shall he set up a sign by it, till the buriers have buried it in the valley of Hamon-gog.
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 And Hamonah shall also be the name of a city. Thus shall they cleanse the land.
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 And thou, son of man, thus saith the Lord GOD: Speak unto the birds of every sort, and to every beast of the field: Assemble yourselves, and come; gather yourselves on every side to My feast that I do prepare for you, even a great feast, upon the mountains of Israel, that ye may eat flesh and drink blood.
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 The flesh of the mighty shall ye eat, and the blood of the princes of the earth shall ye drink; rams, lambs, and goats, bullocks, fatlings of Bashan are they all of them.
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 And ye shall eat fat till ye be full, and drink blood till ye be drunken, of My feast which I have prepared for you.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 And ye shall be filled at My table with horses and horsemen, with mighty men, and with all men of war, saith the Lord GOD.
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 And I will set My glory among the nations, and all the nations shall see My judgment that I have executed, and My hand that I have laid upon them.
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 So the house of Israel shall know that I am the LORD their God, from that day and forward.
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 And the nations shall know that the house of Israel went into captivity for their iniquity, because they broke faith with Me, and I hid My face from them; so I gave them into the hand of their adversaries, and they fell all of them by the sword.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 According to their uncleanness and according to their transgressions did I unto them; and I hid My face from them.
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 Therefore thus saith the Lord GOD: Now will I bring back the captivity of Jacob, and have compassion upon the whole house of Israel; and I will be jealous for My holy name.
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 And they shall bear their shame, and all their breach of faith which they have committed against Me, when they shall dwell safely in their land, and none shall make them afraid;
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 when I have brought them back from the peoples, and gathered them out of their enemies' lands, and am sanctified in them in the sight of many nations.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 And they shall know that I am the LORD their God, in that I caused them to go into captivity among the nations, and have gathered them unto their own land; and I will leave none of them any more there;
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 neither will I hide My face any more from them; for I have poured out My spirit upon the house of Israel, saith the Lord GOD.'
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”