< Ezekiel 35 >

1 Moreover the word of the LORD came unto me, saying:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 'Son of man, set thy face against mount Seir, and prophesy against it,
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
3 and say unto it: Thus saith the Lord GOD: Behold, I am against thee, O mount Seir, and I will stretch out My hand against thee, and I will make thee most desolate.
awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
4 I will lay thy cities waste, and thou shalt be desolate; and thou shalt know that I am the LORD.
Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
5 Because thou hast had a hatred of old, and hast hurled the children of Israel unto the power of the sword in the time of their calamity, in the time of the iniquity of the end;
“Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
6 therefore, as I live, saith the Lord GOD, I will prepare thee unto blood, and blood shall pursue thee; surely thou hast hated thine own blood, therefore blood shall pursue thee.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
7 Thus will I make mount Seir most desolate, and cut off from it him that passeth through and him that returneth.
Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
8 And I will fill his mountains with his slain; in thy hills and in thy valleys and in all thy streams shall they fall that are slain with the sword.
Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
9 I will make thee perpetual desolations, and thy cities shall not return; and ye shall know that I am the LORD.
Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
10 Because thou hast said: These two nations and these two countries shall be mine, and we will possess it; whereas the LORD was there;
“Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
11 therefore, as I live, saith the Lord GOD, I will do according to thine anger and according to thine envy, which thou hast used out of thy hatred against them; and I will make Myself known among them, when I shall judge thee.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
12 And thou shalt know that I the LORD have heard all thy blasphemies which thou hast spoken against the mountains of Israel, saying: They are laid desolate, they are given us to devour.
Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
13 And ye have magnified yourselves against Me with your mouth, and have multiplied your words against Me; I have heard it.
Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
14 Thus saith the Lord GOD: When the whole earth rejoiceth, I will make thee desolate.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
15 As thou didst rejoice over the inheritance of the house of Israel, because it was desolate, so will I do unto thee; thou shalt be desolate, O mount Seir, and all Edom, even all of it; and they shall know that I am the LORD.
Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezekiel 35 >