< Ezekiel 34 >

1 And the word of the LORD came unto me, saying:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 'Son of man, prophesy against the shepherds of Israel, prophesy, and say unto them, even to the shepherds: Thus saith the Lord GOD: Woe unto the shepherds of Israel that have fed themselves! should not the shepherds feed the sheep?
“Iwe mwana wa munthu, yankhula mawu oyimba mlandu abusa a Israeli. Lengeza ndipo uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Tsoka kwa abusa a Israeli amene mumangodzisamala nokha! Kodi abusa sayenera kusamalira nkhosa?
3 Ye did eat the fat, and ye clothed you with the wool, ye killed the fatlings; but ye fed not the sheep.
Mumadya chambiko, mumadziveka zovala zaubweya, ndi kupha nyama zonenepa, koma simusamalira nkhosazo.
4 The weak have ye not strengthened, neither have ye healed that which was sick, neither have ye bound up that which was broken, neither have ye brought back that which was driven away, neither have ye sought that which was lost; but with force have ye ruled over them and with rigour.
Simunalimbitse nkhosa zofowoka, kapena kuchiritsa zodwala, kapena kumanga mabala a nkhosa zopweteka. Simunabweze zosochera kapena kufunafuna zotayika. Munaziweta mozunza ndi mwankhanza.
5 So were they scattered, because there was no shepherd; and they became food to all the beasts of the field, and were scattered.
Kotero zinabalalika chifukwa zinalibe mʼbusa, ndipo pamene zinabalalika zinakhala chakudya cha zirombo zonse zakuthengo.
6 My sheep wandered through all the mountains, and upon every high hill, yea, upon all the face of the earth were My sheep scattered, and there was none that did search or seek.
Nkhosa zanga zinayendayenda mʼmapiri onse ndi mʼzitunda zonse zazitali. Zinabalalika pa dziko lonse lapansi, ndipo palibe amene anazilondola kapena kuzifunafuna.
7 Therefore, ye shepherds, hear the word of the LORD:
“‘Choncho Inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
8 As I live, saith the Lord GOD, surely forasmuch as My sheep became a prey, and My sheep became food to all the beasts of the field, because there was no shepherd, neither did My shepherds search for My sheep, but the shepherds fed themselves, and fed not My sheep;
Pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Wamphamvuzonse, ndithu, nkhosa zanga zinajiwa ndi zirombo zakuthengo, zinasanduka chakudya cha zirombo chifukwa panalibe abusa. Abusa anga sanafunefune nkhosa zanga. Iwo ankangosamala za iwo okha mʼmalo mosamala nkhosa zanga.
9 therefore, ye shepherds, hear the word of the LORD:
Chifukwa chake, inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
10 Thus saith the Lord GOD: Behold, I am against the shepherds; and I will require My sheep at their hand, and cause them to cease from feeding the sheep; neither shall the shepherds feed themselves any more; and I will deliver My sheep from their mouth, that they may not be food for them.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndayipidwa nanu, inu abusa. Ndidzakulandani nkhosa zanga ndipo simudzazidyetsanso. Ndidzakuchotsani pa ntchito ya ubusa kuti musamangodzidyetsa nokha. Ndidzalanditsa nkhosa zanga kukamwa kwanu ndipo simudzazidyanso.
11 For thus saith the Lord GOD: Behold, here am I, and I will search for My sheep, and seek them out.
“‘Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, mwini wakene ndidzazifunafuna nkhosa zanga ndi kuzisamalira.
12 As a shepherd seeketh out his flock in the day that he is among his sheep that are separated, so will I seek out My sheep; and I will deliver them out of all places whither they have been scattered in the day of clouds and thick darkness.
Monga mʼbusa amanka nafunafuna nkhosa zake pamene zina zabalalikira kutali, moteronso Ine ndidzafunafuna nkhosa zanga. Ndidzazipulumutsa kuchoka kumalo onse kumene zinabalalikira pa nthawi yankhungu ndi mdima.
13 And I will bring them out from the peoples, and gather them from the countries, and will bring them into their own land; and I will feed them upon the mountains of Israel, by the streams, and in all the habitable places of the country.
Ndidzazitulutsa pakati pa mitundu ya anthu ndi kuzisonkhanitsa kuchokera ku mayiko ena, ndipo ndidzazibwezera ku dziko lawo. Ndidzaziwetera ku mapiri a Israeli, mʼmbali mwa mitsinje ndi kumalo kumene kumakhala anthu.
14 I will feed them in a good pasture, and upon the high mountains of Israel shall their fold be; there shall they lie down in a good fold, and in a fat pasture shall they feed upon the mountains of Israel.
Ndidzaziwetera kumalo a msipu wabwino. Mapiri okwera a Israeli adzakhala malo azidyetserako. Kumeneko zidzapumula ku abusa abwino a msipu ndipo zizidzadyadi msipu wonenepetsa pa mapiri a Israeli.
15 I will feed My sheep, and I will cause them to lie down, saith the Lord GOD.
Ine mwini wake ndidzaziweta nkhosa zanga ndi kuzilola kuti zipumule. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
16 I will seek that which was lost, and will bring back that which was driven away, and will bind up that which was broken, and will strengthen that which was sick; and the fat and the strong I will destroy, I will feed them in justice.
Ndidzafunafuna zotayika ndi kubweza zosochera. Ndidzamanga mabala a zopweteka ndi kulimbikitsa zofowoka. Koma zonenepa ndi zamphamvu ndidzaziwononga. Ndidzaweta nkhosazo mwachilungamo.
17 And as for you, O My flock, thus saith the Lord GOD: Behold, I judge between cattle and cattle, even the rams and the he-goats.
“‘Kunena za inu, nkhosa zanga, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa, pakati pa nkhosa zazimuna ndi mbuzi zazimuna.
18 Seemeth it a small thing unto you to have fed upon the good pasture, but ye must tread down with your feet the residue of your pasture? and to have drunk of the settled waters, but ye must foul the residue with your feet?
Kodi sikukukwanirani kudya msipu wabwino kuti muzichita kuponderezanso msipu umene simunadyewo? Kodi simukhutira ndi kumwa madzi abwino kuti muzinka mudetsanso madzi otsalawo ndi mapazi anu?
19 And as for My sheep, they eat that which ye have trodden with your feet, and they drink that which ye have fouled with your feet.
Kodi nkhosa zanga zidye zimene mwazipondaponda ndi kumwa madzi amene mwawadetsa ndi mapazi anu?
20 Therefore thus saith the Lord GOD unto them: Behold, I, even I, will judge between the fat cattle and the lean cattle.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Taonani, Ine mwini wake ndidzaweruza pakati pa nkhosa zonenepa ndi nkhosa zowonda.
21 Because ye thrust with side and with shoulder, and push all the weak with your horns, till ye have scattered them abroad;
Popeza zofowoka mumaziwomba ndi kuzikankhira kumbali, ndipo mumazigunda ndi nyanga zanu nʼkuzimwazira kutali,
22 therefore will I save My flock, and they shall no more be a prey; and I will judge between cattle and cattle.
tsono Ine ndidzapulumutsa nkhosa zanga, ndipo sindidzalolanso kuti zijiwe. Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ina ndi nkhosa inanso.
23 And I will set up one shepherd over them, and he shall feed them, even My servant David; he shall feed them, and he shall be their shepherd.
Ndidzaziyikira mʼbusa mmodzi, mtumiki wanga Davide. Iyeyo ndiye azidzazisamala. Adzakhala mʼbusa wawo.
24 And I the LORD will be their God, and My servant David prince among them; I the LORD have spoken.
Ine Yehova ndidzakhala Mulungu wake ndipo mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu pakati pa nkhosazo. Ine Yehova ndayankhula.
25 And I will make with them a covenant of peace, and will cause evil beasts to cease out of the land; and they shall dwell safely in the wilderness, and sleep in the woods.
“‘Ndidzapangana nazo pangano la mtendere. Ndidzachotsa mʼdzikomo zirombo zolusa. Choncho nkhosa zanga zidzakhala mu mtendere mu chipululu ngakhalenso mʼthengo.
26 And I will make them and the places round about My hill a blessing; and I will cause the shower to come down in its season; there shall be showers of blessing.
Ndidzakhazika anthu anga pafupi ndi phiri langa loyera ndipo ndidzawadalitsa. Ndidzawagwetsera mvula pa nthawi yake ndipo idzakhala mvula ya madalitso.
27 And the tree of the field shall yield its fruit, and the earth shall yield her produce, and they shall be safe in their land; and they shall know that I am the LORD, when I have broken the bars of their yoke, and have delivered them out of the hand of those that made bondmen of them.
Mitengo ya mʼminda idzabereka zipatso zake, ndipo nthaka idzakhala ndi zokolola zake. Anthu adzakhala mwamtendere mʼdziko lawo. Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzathyola magoli awo ndi kuwapulumutsa kuchoka mʼmanja mwa amene anawagwira ukapolo.
28 And they shall no more be a prey to the nations, neither shall the beast of the earth devour them; but they shall dwell safely, and none shall make them afraid.
Anthu amitundu ina sadzawafunkhanso ndipo sadzadyedwa ndi zirombo zakuthengo. Adzakhala mwamtendere ndipo palibe amene adzawaopseze.
29 And I will raise up unto them a plantation for renown, and they shall be no more consumed with hunger in the land, neither bear the shame of the nations any more.
Ndidzawapatsa zokolola zochuluka motero kuti sadzavutikanso ndi njala. Anthu a mitundu ina sadzawanyozanso.
30 And they shall know that I the LORD their God am with them, and that they, the house of Israel, are My people, saith the Lord GOD.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wawo ndili nawo pamodzi, ndipo kuti iwo, Aisraeli, ndi anthu anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
31 And ye My sheep, the sheep of My pasture, are men, and I am your God, saith the Lord GOD.'
Inu ndinu nkhosa zanga, nkhosa zimene ndimazidyetsa. Ine ndine Mulungu wanu. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.’”

< Ezekiel 34 >