< Ecclesiastes 8 >
1 Who is as the wise man? and who knoweth the interpretation of a thing? A man's wisdom maketh his face to shine, and the boldness of his face is changed.
Ndani angafanane ndi munthu wanzeru? Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu? Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.
2 I counsel thee: keep the king's command, and that in regard of the oath of God.
Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu.
3 Be not hasty to go out of his presence; stand not in an evil thing; for he doeth whatsoever pleaseth him.
Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho.
4 Forasmuch as the king's word hath power; and who may say unto him: 'What doest thou?'
Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
5 Whoso keepeth the commandment shall know no evil thing; and a wise man's heart discerneth time and judgment.
Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse, ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.
6 For to every matter there is a time and judgment; for the evil of man is great upon him.
Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse, ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.
7 For he knoweth not that which shall be; for even when it cometh to pass, who shall declare it unto him?
Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?
8 There is no man that hath power over the wind to retain the wind; neither hath he power over the day of death; and there is no discharge in war; neither shall wickedness deliver him that is given to it.
Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.
9 All this have I seen, even applied my heart thereto, whatever the work that is done under the sun; what time one man had power over another to his hurt.
Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza.
10 And so I saw the wicked buried, and they entered into their rest; but they that had done right went away from the holy place, and were forgotten in the city; this also is vanity.
Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.
11 Because sentence against an evil work is not executed speedily, therefore the heart of the sons of men is fully set in them to do evil;
Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa.
12 because a sinner doeth evil a hundred times, and prolongeth his days — though yet I know that it shall be well with them that fear God, that fear before Him;
Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu.
13 but it shall not be well with the wicked, neither shall he prolong his days, which are as a shadow, because he feareth not before God.
Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.
14 There is a vanity which is done upon the earth: that there are righteous men, unto whom it happeneth according to the work of the wicked; again, there are wicked men, to whom it happeneth according to the work of the righteous — I said that this also is vanity.
Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino.
15 So I commended mirth, that a man hath no better thing under the sun, than to eat, and to drink, and to be merry, and that this should accompany him in his labour all the days of his life which God hath given him under the sun.
Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.
16 When I applied my heart to know wisdom, and to see the business that is done upon the earth — for neither day nor night do men see sleep with their eyes —
Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku,
17 then I beheld all the work of God, that man cannot find out the work that is done under the sun; because though a man labour to seek it out, yet he shall not find it; yea further, though a wise man think to know it, yet shall he not be able to find it.
pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.