< Ecclesiastes 12 >
1 Remember then thy Creator in the days of thy youth, before the evil days come, and the years draw nigh, when thou shalt say: 'I have no pleasure in them';
Uzikumbukira mlengi wako masiku a unyamata wako, masiku oyipa asanafike, nthawi isanafike pamene udzanena kuti, “Izi sizikundikondweretsa.”
2 Before the sun, and the light, and the moon, and the stars, are darkened, and the clouds return after the rain;
Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala, mwezi ndi nyenyezi zidzada. Mitambo idzabweranso mvula itagwa.
3 In the day when the keepers of the house shall tremble, and the strong men shall bow themselves, and the grinders cease because they are few, and those that look out shall be darkened in the windows,
Nthawi imene manja ako adzanjenjemera, miyendo yako idzafowoka, pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka, ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.
4 And the doors shall be shut in the street, when the sound of the grinding is low; and one shall start up at the voice of a bird, and all the daughters of music shall be brought low;
Makutu ako adzatsekeka, ndipo sudzamva phokoso lakunja; sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo kapena kulira kwa mbalame mmawa.
5 Also when they shall be afraid of that which is high, and terrors shall be in the way; and the almond-tree shall blossom, and the grasshopper shall drag itself along, and the caperberry shall fail; because man goeth to his long home, and the mourners go about the streets;
Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera, amaopa kuyenda mʼmisewu; Mutu umatuwa kuti mbuu, amayenda modzikoka ngati ziwala ndipo chilakolako chimatheratu. Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.
6 Before the silver cord is snapped asunder, and the golden bowl is shattered, and the pitcher is broken at the fountain, and the wheel falleth shattered, into the pit;
Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke, kapena mbale yagolide isanasweke; mtsuko usanasweke ku kasupe, kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.
7 And the dust returneth to the earth as it was, and the spirit returneth unto God who gave it.
Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera, mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.
8 Vanity of vanities, saith Koheleth; all is vanity.
“Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki. “Zonse ndi zopandapake!”
9 And besides that Koheleth was wise, he also taught the people knowledge; yea, he pondered, and sought out, and set in order many proverbs.
Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri.
10 Koheleth sought to find out words of delight, and that which was written uprightly, even words of truth.
Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.
11 The words of the wise are as goads, and as nails well fastened are those that are composed in collections; they are given from one shepherd.
Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi.
12 And furthermore, my son, be admonished: of making many books there is no end; and much study is a weariness of the flesh.
Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi. Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.
13 The end of the matter, all having been heard: fear God, and keep His commandments; for this is the whole man.
Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa: uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake, pakuti umenewu ndiwo udindo wa anthu onse.
14 For God shall bring every work into the judgment concerning every hidden thing, whether it be good or whether it be evil.
Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse, kuphatikizanso zinthu zonse zobisika, kaya zabwino kapena zoyipa.