< Deuteronomy 14 >
1 Ye are the children of the LORD your God: ye shall not cut yourselves, nor make any baldness between your eyes for the dead.
Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
2 For thou art a holy people unto the LORD thy God, and the LORD hath chosen thee to be His own treasure out of all peoples that are upon the face of the earth.
pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
3 Thou shalt not eat any abominable thing.
Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
4 These are the beasts which ye may eat: the ox, the sheep, and the goat,
Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
5 the hart, and the gazelle, and the roebuck, and the wild goat, and the pygarg, and the antelope, and the mountain-sheep.
mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
6 And every beast that parteth the hoof, and hath the hoof wholly cloven in two, and cheweth the cud, among the beasts, that ye may eat.
Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
7 Nevertheless these ye shall not eat of them that only chew the cud, or of them that only have the hoof cloven: the camel, and the hare, and the rock-badger, because they chew the cud but part not the hoof, they are unclean unto you;
Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
8 and the swine, because he parteth the hoof but cheweth not the cud, he is unclean unto you; of their flesh ye shall not eat, and their carcasses ye shall not touch.
Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
9 These ye may eat of all that are in the waters: whatsoever hath fins and scales may ye eat;
Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
10 and whatsoever hath not fins and scales ye shall not eat; it is unclean unto you.
Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
11 Of all clean birds ye may eat.
Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
12 But these are they of which ye shall not eat: the great vulture, and the bearded vulture, and the ospray;
Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
13 and the glede, and the falcon, and the kite after its kinds;
nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
14 and every raven after its kinds;
mtundu uliwonse wa khwangwala,
15 and the ostrich, and the night-hawk, and the sea-mew, and the hawk after its kinds;
kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
16 the little owl, and the great owl, and the horned owl;
kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
17 and the pelican, and the carrion-vulture, and the cormorant;
tsekwe, vuwo, dembo,
18 and the stork, and the heron after its kinds, and the hoopoe, and the bat.
indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
19 And all winged swarming things are unclean unto you; they shall not be eaten.
Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
20 Of all clean winged things ye may eat.
Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
21 Ye shall not eat of any thing that dieth of itself; thou mayest give it unto the stranger that is within thy gates, that he may eat it; or thou mayest sell it unto a foreigner; for thou art a holy people unto the LORD thy God. Thou shalt not seethe a kid in its mother's milk.
Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
22 Thou shalt surely tithe all the increase of thy seed, that which is brought forth in the field year by year.
Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
23 And thou shalt eat before the LORD thy God, in the place which He shall choose to cause His name to dwell there, the tithe of thy corn, of thy wine, and of thine oil, and the firstlings of thy herd and of thy flock; that thou mayest learn to fear the LORD thy God always.
Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
24 And if the way be too long for thee, so that thou art not able to carry it, because the place is too far from thee, which the LORD thy God shall choose to set His name there, when the LORD thy God shall bless thee;
Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
25 then shalt thou turn it into money, and bind up the money in thy hand, and shalt go unto the place which the LORD thy God shall choose.
ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
26 And thou shalt bestow the money for whatsoever thy soul desireth, for oxen, or for sheep, or for wine, or for strong drink, or for whatsoever thy soul asketh of thee; and thou shalt eat there before the LORD thy God, and thou shalt rejoice, thou and thy household.
Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
27 And the Levite that is within thy gates, thou shalt not forsake him; for he hath no portion nor inheritance with thee.
Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
28 At the end of every three years, even in the same year, thou shalt bring forth all the tithe of thine increase, and shall lay it up within thy gates.
Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
29 And the Levite, because he hath no portion nor inheritance with thee, and the stranger, and the fatherless, and the widow, that are within thy gates, shall come, and shall eat and be satisfied; that the LORD thy God may bless thee in all the work of thy hand which thou doest.
kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.