< Amos 7 >
1 Thus the Lord GOD showed me; and, behold, He formed locusts in the beginning of the shooting up of the latter growth; and, lo, it was the latter growth after the king's mowings.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
2 And if it had come to pass, that when they had made an end of eating the grass of the land — so I said: O Lord GOD, forgive, I beseech Thee; how shall Jacob stand? for he is small.
Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
3 The LORD repented concerning this; 'It shall not be', saith the LORD.
Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
4 Thus the Lord GOD showed me; and, behold, the Lord GOD called to contend by fire; and it devoured the great deep, and would have eaten up the land.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
5 Then said I: O Lord GOD, cease, I beseech Thee; how shall Jacob stand? for he is small.
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
6 The LORD repented concerning this; 'This also shall not be', saith the Lord GOD.
Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
7 Thus He showed me; and, behold, the Lord stood beside a wall made by a plumbline, with a plumbline in His hand.
Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
8 And the LORD said unto me: 'Amos, what seest thou?' And I said: 'A plumbline.' Then said the Lord: Behold, I will set a plumbline in the midst of My people Israel; I will not again pardon them any more;
Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
9 And the high places of Isaac shall be desolate, and the sanctuaries of Israel shall be laid waste; and I will rise against the house of Jeroboam with the sword.
“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
10 Then Amaziah the priest of Beth-el sent to Jeroboam king of Israel, saying: 'Amos hath conspired against thee in the midst of the house of Israel; the land is not able to bear all his words.
Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
11 For thus Amos saith: Jeroboam shall die by the sword, and Israel shall surely be led away captive out of his land.'
Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
12 Also Amaziah said unto Amos: 'O thou seer, go, flee thee away into the land of Judah, and there eat bread, and prophesy there;
Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
13 but prophesy not again any more at Beth-el, for it is the king's sanctuary, and it is a royal house.'
Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
14 Then answered Amos, and said to Amaziah: 'I was no prophet, neither was I a prophet's son; but I was a herdman, and a dresser of sycamore-trees;
Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
15 and the LORD took me from following the flock, and the LORD said unto me: Go, prophesy unto My people Israel.
Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
16 Now therefore hear thou the word of the LORD: Thou sayest: Prophesy not against Israel, and preach not against the house of Isaac;
Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
17 Therefore thus saith the LORD: Thy wife shall be a harlot in the city, and thy sons and thy daughters shall fall by the sword, and thy land shall be divided by line; and thou thyself shalt die in an unclean land, and Israel shall surely be led away captive out of his land.'
“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”