< 2 Samuel 22 >
1 And David spoke unto the LORD the words of this song in the day that the LORD delivered him out of the hand of all his enemies, and out of the hand of Saul;
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
2 and he said: The LORD is my rock, and my fortress, and my deliverer;
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
3 The God who is my rock, in Him I take refuge; my shield, and my horn of salvation, my high tower, and my refuge; my saviour, Thou savest me from violence.
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
4 Praised, I cry, is the LORD, and I am saved from mine enemies.
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
5 For the waves of Death compassed me. The floods of Belial assailed me.
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 The cords of Sheol surrounded me; the snares of Death confronted me. (Sheol )
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
7 In my distress I called upon the LORD, yea, I called unto my God; and out of His temple He heard my voice, and my cry did enter into His ears.
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
8 Then the earth did shake and quake, the foundations of heaven did tremble; they were shaken, because He was wroth.
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
9 Smoke arose up in His nostrils, and fire out of His mouth did devour; coals flamed forth from Him.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 He bowed the heavens also, and came down; and thick darkness was under His feet.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 And He rode upon a cherub, and did fly; yea, He was seen upon the wings of the wind.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 And He made darkness pavilions round about Him, gathering of waters, thick clouds of the skies.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 At the brightness before Him coals of fire flamed forth.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
14 The LORD thundered from heaven, and the Most High gave forth His voice.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 And He sent out arrows, and scattered them; lightning, and discomfited them.
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 And the channels of the sea appeared, the foundations of the world were laid bare by the rebuke of the LORD, at the blast of the breath of His nostrils.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
17 He sent from on high, He took me; He drew me out of many waters;
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 He delivered me from mine enemy most strong, from them that hated me, for they were too mighty for me.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 They confronted me in the day of my calamity; but the LORD was a stay unto me.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
20 He brought me forth also into a large place; He delivered me, because He delighted in me.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
21 The LORD rewarded me according to my righteousness; according to the cleanness of my hands hath He recompensed me.
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 For I have kept the ways of the LORD, and have not wickedly departed from my God.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 For all His ordinances were before me; and as for His statutes, I did not depart from them.
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
24 And I was single-hearted toward Him, and I kept myself from mine iniquity.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 Therefore hath the LORD recompensed me according to my righteousness, according to my cleanness in His eyes.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
26 With the merciful Thou dost show Thyself merciful, with the upright man Thou dost show Thyself upright,
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 With the pure Thou dost show myself pure; and with the crooked Thou dost show Thyself subtle.
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 And the afflicted people Thou dost save; but Thine eyes are upon the haughty, that Thou mayest humble them.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 For Thou art my lamp, O LORD; and the LORD doth lighten my darkness.
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 For by Thee I run upon a troop; by my God do I scale a wall.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
31 As for God, His way is perfect; the word of the LORD is tried; He is a shield unto all them that take refuge in Him.
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 For who is God, save the LORD? and who is a Rock, save our God?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 The God who is my strong fortress, and who letteth my way go forth straight;
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
34 Who maketh my feet like hinds', and setteth me upon my high places;
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 Who traineth my hands for war, so that mine arms do bend a bow of brass.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 Thou hast also given me Thy shield of salvation; and Thy condescension hath made me great.
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
37 Thou hast enlarged my steps under me, and my feet have not slipped.
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
38 I have pursued mine enemies, and destroyed them; neither did I turn back till they were consumed.
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 And I have consumed them, and smitten them through, that they cannot arise; yea, they are fallen under my feet.
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 For Thou hast girded me with strength unto the battle; Thou hast subdued under me those that rose up against me.
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 Thou hast also made mine enemies turn their backs unto me; yea, them that hate me, that I might cut them off.
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
42 They looked, but there was none to save; even unto the LORD, but He answered them not.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 Then did I beat them small as the dust of the earth, I did stamp them as the mire of the streets, and did tread them down.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
44 Thou also hast delivered me from the contentions of my people; Thou hast kept me to be the head of the nations; a people whom I have not known serve me.
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45 The sons of the stranger dwindle away before me; as soon as they hear of me, they obey me.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
46 The sons of the stranger fade away, and come halting out of their close places.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
47 The LORD liveth, and blessed be my Rock; and exalted be the God, my Rock of salvation;
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 Even the God that executeth vengeance for me, and bringeth down peoples under me,
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49 And that bringeth me forth from mine enemies; yea, Thou liftest me up above them that rise up against me; Thou deliverest me from the violent man.
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 Therefore I will give thanks unto Thee, O LORD, among the nations, and will sing praises unto Thy name.
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
51 A tower of salvation is He to His king; and showeth mercy to His anointed, to David and to his seed, for evermore.
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”