< 2 Kings 6 >

1 And the sons of the prophets said unto Elisha: 'Behold now, the place where we dwell before thee is too strait for us.
Ana a aneneri anati kwa Elisa, “Taonani malo amene timakhala ndi inu atichepera kwambiri.
2 Let us go, we pray thee, unto the Jordan, and take thence every man a beam, and let us make us a place there, where we may dwell.' And he answered: 'Go ye.'
Tiloleni tipite ku Yorodani kumene aliyense wa ife akadule mtengo umodzi, kuti timange malo woti tizikhalamo.” Ndipo Elisa anati, “Pitani.”
3 And one said: 'Be content, I pray thee, and go with thy servants.' And he answered: 'I will go.'
Mmodzi wa iwo anati, “Chonde mulole kutsagana nawo atumiki anu.” Elisa anayankha kuti, “Ndipita nanu.”
4 So he went with them. And when they came to the Jordan, they cut down wood.
Ndipo anapita nawo. Anapita ku Yorodani nayamba kudula mitengo.
5 But as one was felling a beam, the axe-head fell into the water; and he cried, and said: 'Alas, my master! for it was borrowed.'
Pamene wina ankadula mtengo, nkhwangwa yake inaguluka nigwera mʼmadzi. Iye anafuwula kuti, “Mayo! Mbuye wanga! Popeza ndi yobwereka!”
6 And the man of God said: 'Where fell it?' And he showed him the place. And he cut down a stick, and cast it in thither, and made the iron to swim.
Ndipo munthu wa Mulungu uja anafunsa, “Yagwera pati?” Pamene anamuonetsa malowo, Elisa anadula kamtengo nakaponya pamenepo, ndipo nkhwangwayo inayandama.
7 And he said: 'Take it up to thee.' So he put out his hand, and took it.
Elisa anati, “Itenge.” Ndipo munthuyo anatambalitsa dzanja lake nayitenga.
8 Now the king of Aram warred against Israel; and he took counsel with his servants, saying: 'In such and such a place shall be my camp.'
Tsono mfumu ya ku Aramu inali pa nkhondo ndi Israeli. Itakambirana ndi atsogoleri ake ankhondo inati, “Ndidzamanga misasa yanga pamalo akutiakuti.”
9 And the man of God sent unto the king of Israel, saying: 'Beware that thou pass not such a place; for thither the Arameans are coming down.'
Munthu wa Mulungu anatumiza mawu kwa mfumu ya ku Israeli kuti “Musamale podutsa malo akuti, chifukwa Aaramu akupita kumeneko.”
10 And the king of Israel sent to the place which the man of God told him and warned him of; and he guarded himself there, not once nor twice.
Choncho mfumu ya ku Israeli inatuma anthu kumalo kumene munthu wa Mulunguyo ananena. Nthawi ndi nthawi Elisa ankachenjeza mfumu, kotero kuti ankakhala tcheru ku malo amenewo.
11 And the heart of the king of Aram was sore troubled for this thing; and he called his servants, and said unto them: 'Will ye not tell me which of us is for the king of Israel?'
Zimenezi zinakwiyitsa kwambiri mfumu ya ku Aramu. Mfumuyo inayitanitsa atsogoleri ake ankhondo ndipo inawafunsa kuti, “Kodi simungandiwuze munthu amene pakati pathu pano ali mbali ya mfumu ya ku Israeli?”
12 And one of his servants said: 'Nay, my lord, O king; but Elisha, the prophet that is in Israel, telleth the king of Israel the words that thou speakest in thy bed-chamber.'
Mmodzi mwa atsogoleri a ankhondowo anati, “Palibe ndi mmodzi yemwe pakati pathu, inu mbuye wanga, koma Elisa mneneri amene ali ku Israeli amawuza mfumu ya ku Israeli mawu enieni amene inu mumayankhula ku chipinda kwanu.”
13 And he said: 'Go and see where he is, that I may send and fetch him.' And it was told him, saying: 'Behold, he is in Dothan.'
Choncho mfumu inalamula kuti, “Pitani, kafufuzeni kumene akukhala kuti ine nditume anthu kukamugwira.” Anthuwo anabweretsa mawu oti, “Taonani, Elisa ali ku Dotani.”
14 Therefore sent he thither horses, and chariots, and a great host; and they came by night, and compassed the city about.
Ndipo mfumu inatumizako magaleta ndi akavalo ndiponso gulu lankhondo lamphamvu. Anapita usiku nakawuzungulira mzindawo.
15 And when the servant of the man of God was risen early, and gone forth, behold, a host with horses and chariots was round about the city. And his servant said unto him: 'Alas, my master! how shall we do?'
Mtumiki wa munthu wa Mulungu atadzuka mmamawa ndi kutuluka panja, gulu la ankhondo pamodzi ndi akavalo ndi magaleta anali atazungulira mzindawo. Mtumikiyo anafunsa kuti, “Kalanga mbuye wanga, tidzachita chiyani?”
16 And he answered: 'Fear not: for they that are with us are more than they that are with them.'
Mneneri anamuyankha kuti, “Usachite mantha. Amene ali mbali yathu ndi ambiri kupambana amene ali mbali yawo.”
17 And Elisha prayed, and said: 'LORD, I pray Thee, open his eyes, that he may see.' And the LORD opened the eyes of the young man; and he saw; and, behold, the mountain was full of horses and chariots of fire round about Elisha.
Ndipo Elisa anapemphera kuti, “Inu Yehova tsekulani maso ake kuti aone.” Pamenepo Yehova anatsekula maso a mtumikiyo, ndipo anayangʼana naona kuti phiri lonse linali lodzaza ndi akavalo ndi magaleta a moto atazungulira Elisa.
18 And when they came down to him, Elisha prayed unto the LORD, and said: 'Smite this people, I pray Thee, with blindness.' And He smote them with blindness according to the word of Elisha.
Pamene adaniwo ankabwera kudzalimbana naye, Elisa anapemphera kwa Yehova kuti, “Achititseni khungu anthu awa.” Kotero Yehova anawachititsa khungu monga anapemphera Elisa.
19 And Elisha said unto them: 'This is not the way, neither is this the city; follow me, and I will bring you to the man whom ye seek.' And he led them to Samaria.
Elisa anawawuza ankhondowo kuti, “Njira si imeneyi ndipo mzinda sumenewunso. Tsateni, ndipo ndidzakutengerani kwa munthu amene mukumufunayo.” Ndipo anawatengera ku Samariya.
20 And it came to pass, when they were come into Samaria, that Elisha said: 'LORD, open the eyes of these men, that they may see.' And the LORD opened their eyes, and they saw; and, behold, they were in the midst of Samaria.
Atalowa mu mzinda wa Samariya, Elisa anati, “Yehova tsekulani maso a anthu awa kuti aone.” Choncho Yehova anatsekula maso awo ndipo anangoona kuti ali mʼkati mwenimweni mwa Samariya.
21 And the king of Israel said unto Elisha, when he saw them: 'My father, shall I smite them? shall I smite them?'
Mfumu ya ku Israeli itawaona, inafunsa Elisa kuti, “Abambo anga, kodi ndiwaphe? Kodi ndiwaphe?”
22 And he answered: 'Thou shalt not smite them; hast thou taken captive with thy sword and with thy bow those whom thou wouldest smite? set bread and water before them, that they may eat and drink, and go to their master.'
Elisa anayankha kuti, “Musawaphe. Kodi mungaphe anthu amene munawagwira pogwiritsa ntchito lupanga ndi uta? Apatseni chakudya ndi madzi kuti adye ndi kumwa kenaka apite kwa mbuye wawo.”
23 And he prepared great provision for them; and when they had eaten and drunk, he sent them away, and they went to their master. And the bands of Aram came no more into the land of Israel.
Choncho anawakonzera mphwando lalikulu, ndipo atatsiriza kudya ndi kumwa, anawatumiza kwawo ndipo anabwerera kwa mbuye wawo. Kotero magulu a ankhondo a ku Aramu analeka kuthira nkhondo dziko la Israeli.
24 And it came to pass after this, that Ben-hadad king of Aram gathered all his host, and went up, and besieged Samaria.
Patapita nthawi, Beni-Hadadi mfumu ya Aramu anasonkhanitsa gulu lake lonse la ankhondo, napita kukazungulira mzinda wa Samariya.
25 And there was a great famine in Samaria; and, behold, they besieged it, until an ass's head was sold for fourscore pieces of silver, and the fourth part of a kab of dove's dung for five pieces of silver.
Mu mzinda wa Samariya munali njala yoopsa. Ndipo taonani, Aaramu anazungulira mzindawu kwa nthawi yayitali kotero kuti mutu wa bulu ankawugulitsa ndalama za siliva 80, ndipo magalamu 200 a zitosi za nkhunda ankawagulitsa pa mtengo wa masekeli asanu.
26 And as the king of Israel was passing by upon the wall, there cried a woman unto him, saying: 'Help, my lord, O king.'
Pamene mfumu inkayenda pa khoma la mzindawo, mayi wina anafuwulira mfumuyo kuti, “Thandizeni mbuye wanga mfumu!”
27 And he said: 'If the LORD do not help thee, whence shall I help thee? out of the threshingfloor, or out of the winepress?'
Mfumu inayankha kuti, “Ngati Yehova sakuthandiza iwe, ine thandizo lako ndingalipeze kuti? Kuchokera ku malo opunthira tirigu kodi? Kuchokera kumalo opsinyira mphesa kodi?”
28 And the king said unto her: 'What aileth thee?' And she answered: 'This woman said unto me: Give thy son, that we may eat him to-day, and we will eat my son to-morrow.
Pamenepo mfumuyo inafunsa mayiyo kuti, “Kodi chakuvuta nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Mayi uyu anandiwuza kuti, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye lero, ndipo mawa tidzadya mwana wangayu.’
29 So we boiled my son, and did eat him; and I said unto her on the next day: Give thy son, that we may eat him; and she hath hid her son.'
Choncho tinaphika mwana wanga ndi kumudya. Tsiku lotsatira lakelo ine ndinati, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye,’ koma iye anabisa mwana wakeyo.”
30 And it came to pass, when the king heard the words of the woman, that he rent his clothes — now he was passing by upon the wall — and the people looked, and, behold, he had sackcloth within upon his flesh.
Mfumu itamva mawu a mayiyo, inangʼamba mkanjo wake. Pamene inkayenda pa khoma, anthu anayangʼana, ndipo anaona zovala zamʼkati, pakuti anavala chiguduli.
31 Then he said: 'God do so to me, and more also, if the head of Elisha the son of Shaphat shall stand on him this day.'
Mfumuyo inati, “Mulungu andilange, andilange kwambiri ndikapanda kudula mutu wa Elisa mwana wa Safati lero!”
32 But Elisha sat in his house, and the elders sat with him; and the king sent a man from before him; but ere the messenger came to him, he said to the elders: 'See ye how this son of a murderer hath sent to take away my head? look, when the messenger cometh, shut the door, and hold the door fast against him; is not the sound of his master's feet behind him?'
Tsono Elisa nʼkuti atakhala mʼnyumba mwake, ndipo akuluakulu anali naye limodzi. Mfumu inatuma munthu wina kuti imutsogolere, koma asanafike, Elisa anawuza akuluakuluwo kuti, “Kodi simukuona momwe wopha munthu uja watumizira munthu wina kuti adzadule mutu wanga? Taonani mthengayo akafika, mutseke chitseko ndipo muchigwiritsitse kuti asalowe. Kodi ndikumvawo pambuyo pake si mgugu wa mbuye wake?”
33 And while he yet talked with them, behold, the messenger came down unto him; and the king said: 'Behold, this evil is of the LORD; why should I wait for the LORD any longer?'
Elisa akuyankhulabe ndi anthuwo, taonani, wamthengayo anafika kwa iye. Ndipo mfumu inati, “Mavuto amenewa ndi ochokera kwa Yehova. Kodi nʼchifukwa chiyani ine ndiyenera kudikira thandizo lochokera kwa Yehova?”

< 2 Kings 6 >