< 1 Samuel 26 >
1 And the Ziphites came unto Saul to Gibeah, saying: 'Doth not David hide himself in the hill of Hachilah, which is before Jeshimon?'
Anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ku Gibeya nati, “Davide akubisala ku phiri la Hakila, limene limayangʼanana ndi Yesimoni.”
2 Then Saul arose, and went down to the wilderness of Ziph, having three thousand chosen men of Israel with him, to seek David in the wilderness of Ziph.
Choncho Sauli ananyamuka pamodzi ndi ankhondo ake 3,000 napita ku chipululu cha Zifi kukafunafuna Davide ku chipululuko.
3 And Saul pitched in the hill of Hachilah, which is before Jeshimon, by the way. But David abode in the wilderness, and he saw that Saul came after him into the wilderness.
Sauli anamanga msasa wake mʼmbali mwa njira yopita ku phiri la Hakila moyangʼanana ndi Yesimoni. Koma Davide anali mʼchipululumo. Davide ataona kuti Sauli amamulondola mpaka kumeneko,
4 David therefore sent out spies, and understood that Saul was come of a certainty.
iye anatumiza anthu okazonda ndipo anapeza kuti Sauli wafikadi ndithu.
5 And David arose, and came to the place where Saul had pitched; and David beheld the place where Saul lay, and Abner the son of Ner, the captain of his host; and Saul lay within the barricade, and the people pitched round about him.
Tsono Davide ananyamuka napita kumalo kumene Sauli anamanga misasa. Iye anaona pamene Sauli ndi Abineri mwana wa Neri mkulu wa ankhondo anagona. Sauli anagona mʼkati mwa tenti ndipo asilikali anagona momuzungulira.
6 Then answered David and said to Ahimelech the Hittite, and to Abishai the son of Zeruiah, brother to Joab, saying: 'Who will go down with me to Saul to the camp?' And Abishai said: 'I will go down with thee.'
Ndipo Davide anafunsa Ahimeleki Mhiti ndi Abisai mwana wa Zeruya, mʼbale wa Yowabu kuti, “Ndani adzapita nane ku msasa kwa Sauli?” Abisai anayankha kuti, “Ine ndidzapita nanu.”
7 So David and Abishai came to the people by night; and, behold, Saul lay sleeping within the barricade, with his spear stuck in the ground at his head; and Abner and the people lay round about him.
Choncho Davide ndi Abisai anapita ku misasa ya ankhondowo usiku. Atafika anangopeza Sauli ali gone mu msasa wake mkondo wake atawuzika pansi pafupi ndi mutu wake, Abineri ndi ankhondo onse anali atagona momuzungulira.
8 Then said Abishai to David: 'God hath delivered up thine enemy into thy hand this day; now therefore let me smite him, I pray thee, with the spear to the earth at one stroke, and I will not smite him the second time.'
Abisai anawuza Davide kuti, “Lero Mulungu wapereka mdani wanu mʼmanja mwanu. Tsopano ndiloleni ndimukhomere pansi ndi mkondo wangawu kamodzinʼkamodzi. Sindimulasa kawiri.”
9 And David said to Abishai: 'Destroy him not; for who can put forth his hand against the LORD'S anointed, and be guiltless?'
Koma Davide anamuyankha Abisai kuti, “Usamuphe! Ndani adzapha wodzozedwa wa Yehova ndi kupezeka wosalakwa?
10 And David said: 'As the LORD liveth, nay, but the LORD shall smite him; or his day shall come to die; or he shall go down into battle, and be swept away.
Davide anati, Pali Yehova wamoyo, Yehova mwini ndiye adzamukanthe, mwina tsiku lake lomwalira lidzafika, kapena adzapita ku nkhondo nakaphedwa komweko.
11 The LORD forbid it me, that I should put forth my hand against the LORD'S anointed; but now take, I pray thee, the spear that is at his head, and the cruse of water and let us go.'
Koma Yehova andiletse kuti ndisapweteke wodzozedwa wa Yehova. Tsopano tingotenga mkondo umene uli ku mutu kwakewo ndi botolo la madzilo ndipo tizipita.”
12 So David took the spear and the cruse of water from Saul's head; and they got them away, and no man saw it, nor knew it, neither did any awake; for they were all asleep; because a deep sleep from the LORD was fallen upon them.
Motero Davide anatenga mkondo ndi botolo lamadzi zimene zinali ku mutu kwa Sauli ndipo anachoka. Palibe amene anaona zimenezi kapena kudziwa, ndipo palibenso amene anadzuka. Onse anali mʼtulo, chifukwa Yehova anawagonetsa tulo tofa nato.
13 Then David went over to the other side, and stood on the top of the mountain afar off; a great space being between them.
Pambuyo pake Davide anadutsa nakakwerera mbali ina ya phiri, ndi kuyimirira pamwamba pa phiri patali. Pakati pawo panali mpata waukulu.
14 And David cried to the people, and to Abner the son of Ner, saying: 'Answerest thou not, Abner?' Then Abner answered and said: 'Who art thou that criest to the king?'
Davide anayitana gulu lankhondo ndi Abineri mwana wa Neri nawafunsa kuti, “Kodi sundiyankha ine Abineri?” Abineri anayankha kuti, “Ndiwe yani amene ukuyitana mfumu?”
15 And David said to Abner: 'Art not thou a valiant man? and who is like to thee in Israel? wherefore then hast thou not kept watch over thy lord the king? for there came one of the people in to destroy the king thy lord.
Davide anamufunsa Abineri kuti, “Kodi sindiwe mwamuna? Ndipo wofanana nawe ndani mu Israeli? Nʼchifukwa chiyani sunateteze mbuye wako mfumu? Munthu wina anabwera kumeneko.
16 This thing is not good that thou hast done. As the LORD liveth, ye deserve to die, because ye have not kept watch over your lord, the LORD'S anointed. And now, see, where the king's spear is, and the cruse of water that was at his head.'
Chimene wachita iwe si chabwino. Pali Yehova wamoyo iwe ndi asilikali ako muyenera kufa chifukwa simunateteze mbuye wanu, wodzozedwa wa Yehova. Tayangʼanayangʼana. Uli kuti mkondo wa mfumu ndi botolo lamadzi zimene zinali kumutu kwa mfumu?”
17 And Saul knew David's voice, and said: 'Is this thy voice, my son David?' And David said: 'It is my voice, my lord, O king.'
Sauli anazindikira mawu a Davide ndipo anafunsa kuti, “Kodi amenewa ndi mawu ako Davide mwana wanga?” Davide anayankha, “Inde ndi anga, mbuye wanga mfumu.
18 And he said: 'Wherefore doth my lord pursue after his servant? for what have I done? or what evil is in my hand?
Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mukundilonda ine mtumiki wanu? Kodi ine ndachita chiyani ndipo ndapezeka ndi cholakwa chotani?
19 Now therefore, I pray thee, let my lord the king hear the words of his servant. If it be the LORD that hath stirred thee up against me, let Him accept an offering; but if it be the children of men, cursed be they before the LORD; for they have driven me out this day that I should not cleave unto the inheritance of the LORD, saying: Go, serve other gods.
Tsopano mbuye wanga mfumu tamverani mawu a mtumiki wanu. Ngati ndi Yehova wautsa mtima wanu kuti mundiwukire, ndiye alandire chipepeso. Koma ngati ndi anthu amene achita zimene, ndiye Yehova awatemberere popeza andipirikitsa lero kundichotsa mʼdziko la Yehova, namati, ‘Pita kapembedze milungu ina.’
20 Now therefore, let not my blood fall to the earth away from the presence of the LORD; for the king of Israel is come out to seek a single flea, as when one doth hunt a partridge in the mountains.'
Tsopano musalole kuti magazi anga akhetsedwe kutali ndi Yehova pakuti mfumu ya Israeli yatuluka kudzafunafuna ine nsabwe, monga mmene munthu asakira nkhwali ku mapiri.”
21 Then said Saul: 'I have sinned; return, my son David; for I will no more do thee harm, because my life was precious in thine eyes this day; behold, I have played the fool and erred exceedingly.'
Ndipo Sauli anati, “Ine ndachimwa. Bwerera mwana wanga Davide. Sindidzakuchitanso choyipa popeza lero wauwona moyo wanga ngati wamtengowapatali. Taona, ndachita zauchitsiru ndipo ndachimwa kwambiri.”
22 And David answered and said: 'Behold the king's spear! let then one of the young men come over and fetch it.
Davide anayankha kuti, “Nawu mkondo wanu, mfumu. Tumani mmodzi wa anyamata anu abwere adzatenge.
23 And the LORD will render to every man his righteousness and his faithfulness; forasmuch as the LORD delivered thee into my hand to-day, and I would not put forth my hand against the LORD'S anointed.
Yehova amadalitsa munthu aliyense wolungama ndi wokhulupirika. Yehova anakuperekani lero mʼmanja mwanga, koma ine sindinakhudze wodzozedwa wa Yehova.
24 And, behold, as thy life was much set by this day in mine eyes, so let my life be much set by in the eyes of the LORD, and let Him deliver me out of all tribulation.'
Monga momwe ine lero ndachitira kuwuyesa moyo wanu ngati wamtengowapatali, momwemonso Yehova awuyese moyo wanga wamtengowapatali ndipo andipulumutse mʼmavuto anga onse.”
25 Then Saul said to David: 'Blessed be thou, my son David; thou shalt both do mightily, and shalt surely prevail.' So David went his way, and Saul returned to his place.
Ndipo Sauli anawuza Davide kuti, “Yehova akudalitse iwe Davide mwana wanga. Udzachita zinthu zazikulu ndipo udzapambana.” Choncho Davide anayenda njira yake ndipo Sauli anabwerera kwawo.