< 1 Chronicles 7 >

1 And of the sons of Issachar: Tola, and Puah, Jashub, and Shimron, four.
Ana a Isakara anali awa: Tola, Puwa, Yasubu ndi Simironi ndipo onse analipo anayi.
2 And the sons of Tola: Uzzi and Rephaiah, and Jeriel, and Jahmai, and Ibsam, and Shemuel, heads of their fathers' houses, mighty men of valour according to their generations, even of Tola; their number in the days of David was two and twenty thousand and six hundred.
Ana a Tola ndi awa: Uzi, Refaya, Yerieli, Yahimai, Ibisamu ndi Samueli. Awa anali atsogoleri a mabanja awo. Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide zidzukulu za Tola zomwe zinali anthu odziwa kumenya nkhondo zinalipo 22,600.
3 And the sons of Uzzi: Izrahiah; and the sons of Izrahiah: Michael, and Obadiah, and Joel, Isshiah, five; all of them chief men.
Mwana wa Uzi anali Izirahiya. Ana a Izirahiya anali: Mikayeli, Obadiya, Yoweli ndi Isiya. Onse asanu anali atsogoleri a mabanja.
4 And with them, by their generations, after their fathers' houses, were bands of the host for war, six and thirty thousand; for they had many wives and sons.
Monga mwa chiwerengero cha mabanja awo, panali anthu 36,000 odziwa kumenya nkhondo, pakuti iwo anali ndi akazi ndi ana ambiri.
5 And their brethren among all the families of Issachar, mighty men of valour, reckoned in all by genealogy, were fourscore and seven thousand.
Abale awo onse a mʼbanja la Isakara amene anali odziwa kumenya nkhondo analipo 87,000, olembedwa potsata mibado yawo.
6 The sons of Benjamin: Bela, and Becher, and Jediael, three.
Ana atatu a Benjamini anali awa: Bela, Bekeri ndi Yediaeli.
7 And the sons of Bela: Ezbon, and Uzzi, and Uzziel, and Jerimoth, and Iri, five; heads of fathers' houses, mighty men of valour; and they were reckoned by genealogy twenty and two thousand and thirty and four.
Ana a Bela anali awa: Eziboni, Uzi, Uzieli, Yerimoti ndi Iri. Iwowa anali atsogoleri a mabanja awo ndipo onse pamodzi analipo asanu. Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali anthu 22,034 odziwa kumenya nkhondo.
8 And the sons of Becher: Zemirah, and Joash, and Eliezer, and Elioenai, and Omri, and Jeremoth, and Abijah, and Anathoth, and Alemeth. All these were the sons of Becher.
Ana a Bekeri anali awa: Zemira, Yowasi, Eliezara, Eliyoenai, Omiri, Yeremoti, Abiya, Anatoti ndi Alemeti. Onsewa anali ana a Bekeri.
9 And they were reckoned by genealogy, after their generations, heads of their fathers' houses, mighty men of valour, twenty thousand and two hundred.
Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali atsogoleri a mabanja ndi anthu 20,200 odziwa kumenya nkhondo.
10 And the sons of Jediael: Bilhan; and the sons of Bilhan: Jeush, and Benjamin, and Ehud, and Chenaanah, and Zethan, and Tarshish, and Ahishahar.
Mwana wa Yediaeli anali Bilihani. Ana a Bilihani anali awa: Yeusi, Benjamini, Ehudi, Kenaana, Zetani, Tarisisi ndi Ahisahara.
11 All these were sons of Jediael, even heads of their fathers' houses, mighty men of valour, seventeen thousand and two hundred, that were able to go forth in the host for war.
Ana onsewa a Yediaeli anali atsogoleri a mabanja. Analipo anthu 17,200 amene anali okonzeka kupita ku nkhondo.
12 Shuppim also, and Huppim, the sons of Ir, Hushim, the son of another.
Asupi ndi Ahupi anali zidzukulu za Iri, ndipo Ahusimu anali zidzukulu za Aheri.
13 The sons of Naphtali: Jahziel, and Guni, and Jezer, and Shallum, the sons of Bilhah.
Ana a Nafutali anali awa: Yahazieli, Guni, Yezeri ndi Salumu, zidzukulu za Biliha.
14 The sons of Manasseh: Asriel, whom his wife bore — his concubine the Aramitess bore Machir the father of Gilead;
Ana a Manase anali awa: Asirieli ndi mwana amene anabereka kwa mzikazi wake wa ku Aramu. Mzikazi yemweyo anaberekanso Makiri abambo ake a Giliyadi.
15 and Machir took a wife of Huppim and Shuppim, whose sister's name was Maacah — and the name of the second was Zelophehad; and Zelophehad had daughters.
Makiri anatenga mkazi wa banja la Ahupi ndi Asupi. Mlongo wake anali Maaka. Mwana wake wina anali Zelofehadi, amene anabereka ana aakazi okhaokha.
16 And Maacah the wife of Machir bore a son, and she called his name Peresh; and the name of his brother was Sheresh; and his sons were Ulam and Rekem.
Maaka mkazi wa Makiri anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Perezi. Mʼbale wake anamutcha Seresi, ndipo ana ake anali Ulamu ndi Rakemu.
17 And the sons of Ulam: Bedan. These were the sons of Gilead the son of Machir, the son of Manasseh.
Mwana wa Ulamu anali Bedani. Awa anali ana a Giliyadi mwana wa Makiri, mwana wa Manase.
18 And his sister Hammolecheth bore Ish-hod, and Abiezer, and Mahlah.
Mlongo wake Hamoleketi anabereka Isihodi, Abiezeri ndi Mahila.
19 And the sons of Shemida were Ahian, and Shechem, and Likhi, and Aniam.
Ana a Semida anali: Ahiyani, Sekemu, Likihi ndi Aniyamu.
20 And the sons of Ephraim: Shuthelah — and Bered was his son, and Tahath his son, and Eleadah his son, and Tahath his son,
Ana a Efereimu anali awa: Sutela, Beredi, Tahati, Eliada, Tahati,
21 and Zabad his son, and Shuthelah his son — and Ezer, and Elead, whom the men of Gath that were born in the land slew, because they came down to take away their cattle.
Zabadi, Sutela. Ezeri ndi Eladi anaphedwa ndi anthu a ku Gati, pamene anabwera kudzalanda zoweta zawo.
22 And Ephraim their father mourned many days, and his brethren came to comfort him.
Efereimu, abambo awo, anawalira masiku ambiri, ndipo abale ake anabwera kudzamutonthoza.
23 And he went in to his wife, and she conceived, and bore a son, and he called his name Beriah, because it went evil with his house.
Kenaka anagona ndi mkazi wake, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Beriya, chifukwa tsoka linagwera banja lake.
24 And his daughter was Sheerah, who built Beth-horon the nether and the upper, and Uzzen-sheerah.
Mwana wake wamkazi anali Seera, amene anamanga mzinda wa Beti-Horoni Wakumunsi, Wakumtunda kudzanso Uzeni-Seera.
25 And Rephah was his son, and Resheph, and Telah his son, and Tahan his son;
Mwana wina wa Efereimu anali Refa amene zidzukulu zake zinali Resefu, Tela, Tahani,
26 Ladan his son, Ammihud his son, Elishama his son;
Ladani, Amihudi, Elisama,
27 Nun his son, Joshua his son.
Nuni ndi Yoswa.
28 And their possessions and habitations were Beth-el and the towns thereof, and eastward Naaran, and westward Gezer, with the towns thereof; Shechem also and the towns thereof, unto Aiah and the towns thereof;
Malo amene ankakhala anali Beteli ndi midzi yozungulira, cha kummawa kunali Naarani, Gezeri ndi midzi yake ya kumadzulo ndi Sekemu ndi midzi yake mpaka ku Aya ndi midzi yake.
29 and by the borders of the children of Manasseh, Beth-shean and the towns thereof, Taanach and the towns thereof, Megiddo and the towns thereof, Dor and the towns thereof. In these dwelt the children of Joseph the son of Israel.
Mʼmbali mwa malire a Manase munali Beti-Seani, Taanaki, Megido ndi Dori, pamodzi ndi midzi yake. Zidzukulu za Yosefe mwana wa Israeli zimakhala mʼmizinda imeneyi.
30 The sons of Asher: Imnah, and Ishvah, and Ishvi, and Beriah, and Serah their sister.
Ana a Aseri anali awa: Imuna, Isiva, Isivi ndi Beriya. Mlongo wawo anali Sera.
31 And the sons of Beriah: Heber, and Malchiel, who was the father of Birzaith.
Ana a Beriya anali awa: Heberi ndi Malikieli amene anabereka Birizaiti.
32 And Heber begot Japhlet, and Shomer, and Hotham, and Shua their sister.
Heberi anabereka Yafuleti, Someri, Hotamu ndi Suwa, mlongo wawo.
33 And the sons of Japhlet: Pasach, and Bimhal, and Asvath. These are the children of Japhlet.
Ana a Yafuleti anali awa: Pasaki, Bimuhali ndi Asivati. Awa anali ana a Yafuleti.
34 And the sons of Shemer: Ahi, and Rohgah, and Hubbah, and Aram.
Ana a Someri anali awa: Ahi, Rohiga, Yehuba ndi Aramu.
35 And the sons of Helem his brother: Zophah, and Imna, and Shelesh, and Amal.
Ana a mʼbale wake Helemu anali awa: Zofa, Imuna, Selesi ndi Amali.
36 The sons of Zophah: Suah, and Harnepher, and Shaul, and Beri, and Imrah;
Ana a Zofa anali awa: Suwa, Harineferi, Suwali, Beri, Imula,
37 Bezer, and Hod, and Shamma, and Shilsha, and Ithran, and Beera.
Bezeri, Hodi, Sama, Silisa, Itirani ndi Bera.
38 And the sons of Jether: Jephunneh, and Pispa, and Ara.
Ana a Yeteri anali awa: Yefune, Pisipa ndi Ara.
39 And the sons of Ulla: Arah, and Hanniel, and Rizia.
Ana a Ula anali awa: Ara, Hanieli ndi Riziya.
40 All these were the children of Asher, heads of the fathers' houses, choice and mighty men of valour, chief of the princes. And the number of them reckoned by genealogy for service in war was twenty and six thousand men.
Onsewa anali zidzukulu za Aseri, atsogoleri a mabanja, anthu omveka, ankhondo olimba mtima, ndi akuluakulu pakati pa atsogoleri anzawo. Chiwerengero cha anthu odziwa kumenya nkhondo chomwe chinalembedwa chinali 26,000.

< 1 Chronicles 7 >