< 1 Chronicles 2 >
1 These are the sons of Israel: Reuben, Simeon, Levi, and Judah, Issachar, and Zebulun;
Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
2 Dan, Joseph, and Benjamin, Naphtali, Gad, and Asher.
Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
3 The sons of Judah: Er, and Onan, and Shelah; which three were born unto him of Bath-shua the Canaanitess. And Er, Judah's first-born, was wicked in the sight of the LORD; and He slew him.
Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
4 And Tamar his daughter-in-law bore him Perez and Zerah. All the sons of Judah were five.
Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
5 The sons of Perez: Hezron, and Hamul.
Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
6 And the sons of Zerah: Zimri, and Ethan, and Heman, and Calcol, and Dara: five of them in all.
Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
7 And the sons of Carmi: Achar, the troubler of Israel, who committed a trespass concerning the devoted thing.
Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
8 And the sons of Ethan: Azariah.
Mwana wa Etani anali Azariya.
9 The sons also of Hezron, that were born unto him: Jerahmeel, and Ram, and Chelubai.
Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
10 And Ram begot Amminadab; and Amminadab begot Nahshon, prince of the children of Judah;
Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
11 and Nahshon begot Salma, and Salma begot Boaz;
Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
12 and Boaz begot Obed, and Obed begot Jesse;
Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
13 and Jesse begot his first-born Eliab, and Abinadab the second, and Shimea the third;
Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
14 Nethanel the fourth, Raddai the fifth;
wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
15 Ozem the sixth, David the seventh.
wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
16 And their sisters were Zeruiah and Abigail. And the sons of Zeruiah: Abishai, and Joab, and Asahel, three.
Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
17 And Abigail bore Amasa; and the father of Amasa was Jether the Ishmaelite.
Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
18 And Caleb the son of Hezron begot children of Azubah his wife — and of Jerioth — and these were her sons: Jesher, and Shobab, and Ardon.
Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
19 And Azubah died, and Caleb took unto him Ephrath, who bore him Hur.
Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
20 And Hur begot Uri, and Uri begot Bezalel.
Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
21 And afterward Hezron went in to the daughter of Machir the father of Gilead; whom he took to wife when he was threescore years old; and she bore him Segub.
Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
22 And Segub begot Jair, who had three and twenty cities in the land of Gilead.
Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
23 And Geshur and Aram took Havvoth-jair from them, with Kenath, and the villages thereof, even threescore cities. All these were the sons of Machir the father of Gilead.
(Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
24 And after that Hezron was dead in Caleb-ephrath, then Abiah Hezron's wife bore him Ashhur the father of Tekoa.
Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
25 And the sons of Jerahmeel the first-born of Hezron were Ram the first-born, and Bunah, and Oren, and Ozem, Ahijah.
Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
26 And Jerahmeel had another wife, whose name was Atarah; she was the mother of Onam.
Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
27 And the sons of Ram the first-born of Jerahmeel were Maaz, and Jamin, and Eker.
Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
28 And the sons of Onam were Shammai, and Jada; and the sons of Shammai: Nadab, and Abishur.
Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
29 And the name of the wife of Abishur was Abihail; and she bore him Ahban, and Molid.
Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
30 And the sons of Nadab: Seled, and Appaim; but Seled died without children.
Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
31 And the sons of Appaim: Ishi. And the sons of Ishi: Sheshan. And the sons of Sheshan: Ahlai.
Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
32 And the sons of Jada the brother of Shammai: Jether, and Jonathan: and Jether died without children.
Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
33 And the sons of Jonathan: Peleth, and Zaza. These were the sons of Jerahmeel.
Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
34 Now Sheshan had no sons, but daughters. And Sheshan had a servant, an Egyptian, whose name was Jarha.
Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
35 So Sheshan gave his daughter to Jarha his servant to wife; and she bore him Attai.
Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
36 And Attai begot Nathan, and Nathan begot Zabad;
Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
37 and Zabad begot Ephlal, and Ephlal begot Obed;
Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
38 and Obed begot Jehu, and Jehu begot Azariah;
Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
39 and Azariah begot Helez, and Helez begot Eleasah;
Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
40 and Eleasah begot Sisamai, and Sisamai begot Shallum;
Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
41 and Shallum begot Jekamiah, and Jekamiah begot Elishama.
Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
42 And the sons of Caleb the brother of Jerahmeel were Mesha his first-born, who was the father of Ziph, and the sons of Mareshah the father of Hebron.
Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
43 And the sons of Hebron: Korah, and Tappuah, and Rekem, and Shema.
Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
44 And Shema begot Raham, the father of Jorkeam; and Rekem begot Shammai.
Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
45 And the son of Shammai was Maon; and Maon was the father of Beth-zur.
Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
46 And Ephah, Caleb's concubine, bore Haran, and Moza, and Gazez; and Haran begot Gazez.
Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
47 And the sons of Jahdai: Regem, and Jotham, and Geshan, and Pelet, and Ephah, and Shaaph.
Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
48 Maacah, Caleb's concubine, bore Sheber and Tirhanah.
Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
49 And the wife of Shaaph the father of Madmannah bore Sheva the father of Machbenah and the father of Gibea. And the daughter of Caleb was Achsah.
Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
50 These were the sons of Caleb. The sons of Hur the first-born of Ephrath: Shobal the father of Kiriath-jearim;
Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
51 Salma the father of Beth-lehem, Hareph the father of Beth-gader.
Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
52 And Shobal the father of Kiriath-jearim had sons: Haroeh, and half of the Menuhoth.
Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
53 And the families of Kiriath-jearim: the Ithrites, and the Puthites, and the Shumathites, and the Mishraites; of them came the Zorathites, and the Eshtaolites.
ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
54 The sons of Salma: Beth-lehem, and the Netophathites, Atroth-beth-joab, and half of the Manahathites, the Zorites.
Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
55 And the families of scribes that dwelt at Jabez: the Tirathites, the Shimeathites, the Sucathites. These are the Kenites that came of Hammath, the father of the house of Rechab.
ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.