< 1 Chronicles 13 >

1 And David consulted with the captains of thousands and of hundreds, even with every leader.
Davide anakambirana ndi akuluakulu ake, atsogoleri a anthu 1,000 ndi atsogoleri a anthu 100.
2 And David said unto all the assembly of Israel: 'If it seem good unto you, and if it be of the LORD our God, let us send abroad everywhere unto our brethren that are left in all the land of Israel, and with them to the priests and Levites that are in their cities that have open land about them, that they may gather themselves unto us;
Ndipo anati kwa gulu lonse la Israeli, “Ngati kukukomerani komanso ngati chili chifuniro cha Yehova Mulungu wathu, tiyeni titumize uthenga kulikonse kumene kuli abale athu ena onse ku dziko lonse la Israeli ndiponso kwa ansembe ndi Alevi amene ali nawo mʼmidzi yawo ndi madera odyetsera ziweto, kuti abwere adzakhale nafe.
3 and let us bring back the ark of our God to us; for we sought not unto it in the days of Saul.'
Tiyeni tibweretsenso Bokosi la Mulungu wathu kuno kwathu, pakuti nthawi ya Sauli sitinafunse za bokosili.”
4 And all the assembly said that they would do so; for the thing was right in the eyes of all the people.
Gulu lonse linavomereza izi, pakuti anthu onse anaona kuti kunali kofunika kutero.
5 So David assembled all Israel together, from Shihor the brook of Egypt even unto the entrance of Hamath, to bring the ark of God from Kiriath-jearim.
Kotero Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse, kuchokera ku mtsinje wa Sihori ku Igupto mpaka ku Lebo Hamati, kuti abweretse Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriati-Yearimu.
6 And David went up, and all Israel, to Baalah, that is, to Kiriath-jearim, which belonged to Judah, to bring up from thence the ark of God, the LORD that sitteth upon the cherubim, whereon is called the Name.
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse anapita ku Baalahi (Kiriati-Yearimu) ku Yuda kukatenga Bokosi la Yehova Mulungu, amene amakhala pakati pa akerubi. Limeneli ndiye Bokosi la Chipangano lomwe limadziwika ndi Dzina lake.
7 And they set the ark of God upon a new cart, and brought it out of the house of Abinadab; and Uzza and Ahio drove the cart.
Iwo anachotsa Bokosi la Mulungu ku nyumba ya Abinadabu pa ngolo yatsopano. Uza ndi Ahiyo ndiwo ankayendetsa ngoloyo.
8 And David and all Israel played before God with all their might; even with songs, and with harps, and with psalteries, and with timbrels, and with cymbals, and with trumpets.
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse ankakondwerera ndi mphamvu zawo zonse pamaso pa Mulungu, poyimba nyimbo pogwiritsa ntchito azeze, apangwe, matambolini, maseche ndi malipenga.
9 And when they came unto the threshing-floor of Chidon, Uzza put forth his hand to hold the ark; for the oxen stumbled.
Atafika pa malo opunthira tirigu ku Kidoni, Uza anatambalitsa dzanja lake kuti agwire bokosilo, chifukwa ngʼombe zinkafuna kugwa.
10 And the anger of the LORD was kindled against Uzza, and He smote him, because he put forth his hand to the ark; and there he died before God.
Yehova anapsera mtima Uza ndipo anamukantha chifukwa chogwira bokosilo. Choncho iyeyo anafera pomwepo pamaso pa Mulungu.
11 And David was displeased, because the LORD had broken forth upon Uzza; and that place was called Perez-uzza unto this day.
Ndipo Davide anakhumudwa chifukwa Yehova anakantha Uza ndipo mpaka lero malowo amatchedwa Perezi Uza.
12 And David was afraid of God that day, saying: 'How shall I bring the ark of God home to me?'
Tsiku limenelo Davide anachita mantha ndi Mulungu ndipo anafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu lingafike bwanji kwathu?”
13 So David removed not the ark unto him into the city of David, but carried it aside into the house of Obed-edom the Gittite.
Iye sanapitenso nalo Bokosi la Mulungu ku Mzinda wa Davide. Mʼmalo mwake anapita nalo ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti.
14 And the ark of God remained with the family of Obed-edom in his house three months; and the LORD blessed the house of Obed-edom, and all that he had.
Ndipo Bokosi la Mulungu linakhala mʼbanja la Obedi-Edomu mʼnyumba mwake kwa miyezi itatu ndipo Yehova anadalitsa nyumba yake ndi chilichonse chimene anali nacho.

< 1 Chronicles 13 >