< 1 John 1 >
1 THAT which was from the beginning, which we have seen with our eyes, which we have gazed upon, and our hands have handled of the word of life;
Tikukulalikirani za Mawu a moyo amene analipo kuyambira pachiyambi, amene tinawamva, amene tinawaona ndi maso athu, amene tinawapenyetsetsa, ndipo tinawakhudza ndi manja athu.
2 (for the life was manifested, and we have beheld it, and bear testimony, and declare unto you that life eternal, which was with the Father, and was manifested to us; ) (aiōnios )
Moyowo unaoneka, tinawuona ndipo tikuchitira umboni. Tikukulalikirani za moyo wosatha umene unali ndi Atate ndipo unaonekera kwa ife. (aiōnios )
3 that which we have seen and heard, declare we to you, that ye also may have communion with us: and indeed our communion is with the Father, and with his Son Jesus Christ.
Tikukulalikirani chimene tinachiona ndi kumva, kuti inuyo muyanjane nafe. Kuyanjana kwathu, tikuyanjana ndi Atate ndiponso ndi Mwana wawo, Yesu Khristu.
4 And these things write we unto you, that your joy may be complete.
Tikukulemberani zimenezi kuti chimwemwe chathu chikhale chathunthu.
5 And this is the promise which we have heard from him, and declare unto you, that God is light, and that darkness in him there is none.
Uthenga umene tinamva kwa Iye ndipo tikuwulalikira kwa inu ndi uwu: Mulungu ndiye kuwunika ndipo mwa Iye mulibe mdima konse.
6 If we say that we have communion with him, and walk in darkness, we lie, and practise not the truth:
Tikanena kuti timayanjana naye, koma nʼkumayendabe mu mdima, tikunama ndipo sitikuchita choonadi.
7 but if we walk in the light, as he is himself in the light, we have communion with each other, and the blood of Jesus Christ his Son cleanseth us from all sin.
Koma tikamayenda mʼkuwunika, monga Iye ali mʼkuwunika, pamenepo timayanjana wina ndi mnzake, ndipo magazi a Yesu, Mwana wake, amatitsuka ndi kutichotsera tchimo lililonse.
8 If we say that we have no sin, we deceive ourselves, and the truth is not in us.
Tikanena kuti tilibe tchimo, tikudzinyenga tokha ndipo mwa ife mulibe choonadi.
9 If we confess our sins, faithful is he and righteous to forgive us our sins, and to cleanse us from all unrighteousness.
Koma tikavomereza machimo athu, Iye ndi wokhulupirika ndi wolungama ndipo adzatikhululukira machimo athu, nadzatiyeretsa ndi kutichotsera chosalungama chilichonse.
10 If we say that we have not sinned, we make him a liar, and his word is not in us.
Ife tikanena kuti sitinachimwe, tikumutenga Mulungu kukhala wonama, ndipo Mawu ake sali mwa ife.