< Zechariah 4 >
1 And the Angel that talked with mee, came againe and waked mee, as a man that is raysed out of his sleepe,
Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
2 And saide vnto me, What seest thou? And I said, I haue looked, and beholde, a candlesticke all of gold with a bowle vpon the toppe of it, and his seuen lampes therein, and seuen pipes to the lampes, which were vpon the toppe thereof.
Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
3 And two oliue trees ouer it, one vpon the right side of the bowle, and the other vpon the left side thereof.
Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
4 So I answered, and spake to the Angel that talked with me, saying, What are these, my Lord?
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
5 Then the Angel that talked with mee, answered and said vnto me, Knowest thou not what these be? And I said, No, my Lord.
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
6 Then he answered and spake vnto me, saying, This is the word of the Lord vnto Zerubbabel, saying, Neither by an armie nor strength, but by my Spirit, saith the Lord of hostes.
Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
7 Who art thou, O great mountaine, before Zerubbabel? thou shalt be a plaine, and he shall bring foorth the head stone thereof, with shoutings, crying, Grace, grace vnto it.
“Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
8 Moreouer, the word of the Lord came vnto me, saying,
Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
9 The handes of Zerubbabel haue layde the foundation of this house: his handes shall also finish it, and thou shalt knowe that the Lord of hostes hath sent me vnto you.
“Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
10 For who hath despised the day of the small thinges? but they shall reioyce, and shall see the stone of tinne in the hand of Zerubbabel: these seuen are the eyes of the Lord, which go thorow the whole world.
“Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
11 Then answered I, and said vnto him, What are these two oliue trees vpon the right and vpon the left side thereof?
Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
12 And I spake moreouer, and said vnto him, What bee these two oliue branches, which thorowe the two golden pipes emptie themselues into the golde?
Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
13 And hee answered me, and saide, Knowest thou not what these bee? And I sayde, No, my Lord.
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
14 Then said he, These are the two oliue branches, that stand with the ruler of the whole earth.
Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”