< Zechariah 10 >

1 Aske you of the Lord raine in the time of the latter raine: so shall the Lord make white cloudes, and giue you showers of raine, and to euery one grasse in the field.
Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira; ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula. Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu, ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.
2 Surely the idols haue spoken vanitie, and the southsayers haue seene a lye, and the dreamers haue tolde a vaine thing: they comfort in vaine: therefore they went away as sheepe: they were troubled, because there was no shepheard.
Mafano amayankhula zachinyengo, owombeza mawula amaona masomphenya abodza; amafotokoza maloto onama, amapereka chitonthozo chopandapake. Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika chifukwa chosowa mʼbusa.
3 My wrath was kindled against the shepherdes, and I did visite the goates: but the Lord of hostes will visite his flocke the house of Iudah, and will make them as his beautifull horse in the battell.
“Ine ndawakwiyira kwambiri abusa, ndipo ndidzalanga atsogoleri; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira nkhosa zake, nyumba ya Yuda, ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.
4 Out of him shall the corner come foorth: out of him the nayle, out of him ye bowe of battell, and out of him euery appointer of tribute also.
Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya, mudzachokera chikhomo cha tenti, mudzachokera uta wankhondo, mudzachokera mtsogoleri aliyense.
5 And they shalbe as the mightie men, which treade downe their enemies in the mire of the streetes in the battell, and they shall fight, because the Lord is with them, and the riders on horses shall be confounded.
Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo. Chifukwa Yehova adzakhala nawo, adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.
6 And I will strengthen the house of Iudah, and I will preserue the house of Ioseph, and I wil bring them againe, for I pitie them: and they shall be as though I had not cast them off: for I am the Lord their God, and will heare them.
“Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe. Ndidzawabwezeretsa chifukwa ndawamvera chisoni. Adzakhala ngati kuti sindinawakane, chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo ndipo ndidzawayankha.
7 And they of Ephraim shall be as a gyant, and their heart shall reioyce as thorowe wine: yea, their children shall see it, and be glad: and their heart shall reioyce in the Lord.
Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo. Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala; mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.
8 I will hisse for them, and gather them: for I haue redeemed them: and they shall encrease, as they haue encreased.
Ndidzaliza mluzu ndi kuwasonkhanitsa pamodzi. Ndithu ndawawombola; adzachulukana ngati poyamba paja.
9 And I will sowe them among the people, and they shall remember me in farre countreys: and they shall liue with their children and turne againe.
Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu, koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira. Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka, ndipo adzabwerera.
10 I will bring them againe also out of the land of Egypt, and gather them out of Asshur: and I will bring them into the land of Gilead, and Lebanon, and place shall not be found for them.
Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya. Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni, mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.
11 And he shall goe into the sea with affliction, and shall smite the waues in the sea, and all the depthes of the riuer shall drye vp: and the pride of Asshur shall be cast downe, and the scepter of Egypt shall depart away.
Adzawoloka nyanja ya masautso; nyanja yokokoma idzagonja ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa. Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.
12 And I will strengthen them in the Lord, and they shall walke in his Name, sayth the Lord.
Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova ndipo adzayenda mʼdzina lake,” akutero Yehova.

< Zechariah 10 >