< Revelation 11 >
1 Then was giuen me a reede, like vnto a rod, and the Angel stoode by, saying, Rise and mete the Temple of God, and the altar, and them that worship therein.
Ndinapatsidwa bango longa ndodo yoyezera ndipo ndinawuzidwa kuti, “Pita, kayeze Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, ndipo ukawerenge anthu opembedza mʼNyumbamo.
2 But the court which is without the temple cast out, and mete it not: for it is giuen vnto the Gentiles, and the holy citie shall they treade vnder foote, two and fourtie moneths.
Koma bwalo lakunja ulisiye, usaliyeze chifukwa linaperekedwa kwa a mitundu ina. Iwo adzawupondereza mzinda woyerawo kwa miyezi 42.
3 But I wil giue power vnto my two witnesses, and they shall prophecie a thousande two hundreth and threescore dayes, clothed in sackcloth.
Ndipo ndidzapereka mphamvu kwa mboni zanga ziwiri, zitavala ziguduli, ndipo kwa masiku 1,260 zidzakhala zikulalikira.”
4 These are two oliue trees, and two candlestickes, standing before the God of the earth.
Mboni ziwirizo ndi mitengo iwiri ya olivi ndi zoyikapo nyale ziwiri zija zimene zili pamaso pa Ambuye wa dziko lapansi.
5 And if any man wil hurt them, fire proceedeth out of their mouthes, and deuoureth their enemies: for if any man would hurt the, thus must he be killed.
Ngati wina atafuna kuzipweteka mbonizo, moto umatuluka mʼkamwa mwawo ndikuwononga adani awo.
6 These haue power to shut heauen, that it raine not in the dayes of their prophecying, and haue power ouer waters to turne them into blood, and to smite the earth with all maner plagues, as often as they will.
Mbonizo zili ndi mphamvu yomanga mvula kuti isagwe pa nthawi imene akulalikirayo; ndipo zili ndi mphamvu yosanduliza madzi kukhala magazi ndi yokantha dziko lapansi ndi miliri ya mitundumitundu nthawi iliyonse imene zingafune.
7 And when they haue finished their testimonie, the beast that commeth out of the bottomlesse pit, shall make warre against them, and shall ouercome them, and kill them. (Abyssos )
Tsono zikadzatsiriza umboni wawowo, chirombo chotuluka mʼChidzenje chakuya chija chidzachita nawo nkhondo nʼkuzigonjetsa mpaka kuzipha. (Abyssos )
8 And their corpses shall lie in the streetes of the great citie, which spiritually is called Sodom and Egypt, where our Lord also was crucified.
Mitembo yawo idzakhala ili gone pabwalo la mu mzinda waukulu umene mozimbayitsa umatchedwa Sodomu ndi Igupto, kumenenso Ambuye wawo anapachikidwako.
9 And they of the people and kinreds, and tongues, and Gentiles shall see their corpses three dayes and an halfe, and shall not suffer their carkeises to be put in graues.
Kwa masiku atatu ndi theka, anthu ochokera ku mtundu uliwonse, fuko lililonse, chiyankhulo chilichonse ndi dziko lililonse, azidzayangʼanitsitsa mitembo yawoyo koma adzakana kuyikwirira.
10 And they that dwell vpon the earth, shall reioyce ouer them and be glad, and shall sende giftes one to an other: for these two Prophets vexed them that dwelt on the earth.
Anthu okhala pa dziko lapansi adzasangalala nazo zimenezi. Adzachita chikondwerero ndi kutumizirana mphatso, chifukwa aneneri awiri amenewa ankasautsa anthu okhala pa dziko lapansi.
11 But after three dayes and an halfe, the spirit of life comming from God, shall enter into them, and they shall stande vp vpon their feete: and great feare shall come vpon them which sawe them.
Koma patapita masiku atatu ndi theka aja, mpweya wopatsa moyo wochoka kwa Mulungu unalowa mwa aneneriwo, ndipo anayimirira, ndipo amene anawaona anachita mantha aakulu.
12 And they shall heare a great voyce from heauen, saying vnto them, Come vp hither. And they shall ascend vp to heauen in a cloude, and their enemies shall see them.
Kenaka aneneri aja anamva mawu ofuwula ochokera kumwamba owawuza kuti, “Bwerani kuno.” Ndipo anapitadi kumwamba mu mtambo adani awo aja akuwaona.
13 And the same houre shall there bee a great earthquake, and the tenth part of the citie shall fall, and in the earthquake shalbe slaine in nomber seuen thousande: and the remnant were sore feared, and gaue glorie to the God of heauen.
Nthawi yomweyo panachitika chivomerezi choopsa mwakuti chigawo chimodzi cha magawo khumi a mzinda chinagwa. Anthu 7,000 anaphedwa ndi chivomerezicho, ndipo opulumukawo anachita mantha kwambiri nayamba kutamanda Mulungu wakumwamba.
14 The second woe is past, and beholde, the third woe will come anon.
Tsoka lachiwiri lapita; koma tsoka lachitatu likubwera posachedwapa.
15 And the seuenth Angell blewe the trumpet, and there were great voyces in heauen, saying, The kingdomes of this worlde are our Lordes, and his Christes, and he shall reigne for euermore. (aiōn )
Mngelo wachisanu ndi chiwiri anawomba lipenga lake, ndipo kumwamba kunamveka mawu ofuwula amene anati, “Ufumu wa dziko lapansi uli mʼmanja mwa Ambuye athu ndi Khristu wake uja, ndipo adzalamulira mpaka muyaya.” (aiōn )
16 Then the foure and twentie Elders, which sate before God on their seates, fell vpon their faces, and worshipped God,
Ndipo akuluakulu 24 aja okhala pa mipando yawo yaufumu pamaso pa Mulungu, anadzigwetsa chafufumimba napembedza Mulungu
17 Saying, We giue thee thankes, Lord God almightie, Which art, and Which wast, and Which art to come: for thou hast receiued thy great might, and hast obteined thy kingdome.
Iwo anati, “Ife tikuyamika Inu Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse, amene mulipo ndipo munalipo, chifukwa mwaonetsa mphamvu yanu yayikulu, ndipo mwayamba kulamulira.
18 And the Gentiles were angrie, and thy wrath is come, and the time of the dead, that they shoulde be iudged, and that thou shouldest giue reward vnto thy seruants the Prophets, and to the Saintes, and to them that feare thy Name, to small and great, and shouldest destroy them, which destroy the earth.
A mitundu ina anapsa mtima; koma yafika nthawi yoonetsa mkwiyo. Nthawi yakwana yoweruza anthu akufa, yopereka mphotho kwa atumiki anu, aneneri, anthu oyera mtima anu ndi amene amaopa dzina lanu, wamngʼono pamodzi ndi wamkulu yemwe. Yafika nthawi yowononga amene awononga dziko lapansi.”
19 Then the Temple of God was opened in heauen, and there was seene in his Temple the Arke of his couenant: and there were lightnings, and voyces, and thundrings, and earthquake, and much haile.
Pamenepo anatsekula Nyumba ya Mulungu kumwamba ndipo mʼkati mwake munaoneka Bokosi la Chipangano. Kenaka kunachita mphenzi, phokoso, mabingu, chivomerezi ndipo kunachita mkuntho wamatalala akuluakulu.