< Psalms 98 >

1 A Psalme. Sing vnto the Lord a newe song: for hee hath done marueilous things: his right hand, and his holy arme haue gotten him the victorie.
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
2 The Lord declared his saluation: his righteousnes hath he reueiled in the sight of ye nations.
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
3 He hath remembred his mercy and his trueth toward the house of Israel: all the ends of the earth haue seene the saluation of our God.
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
4 All the earth, sing ye loude vnto the Lord: crie out and reioyce, and sing prayses.
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
5 Sing prayse to the Lord vpon the harpe, euen vpon the harpe with a singing voyce.
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
6 With shalmes and sound of trumpets sing loude before the Lord the King.
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
7 Let the sea roare, and all that therein is, the world, and they that dwell therein.
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
8 Let the floods clap their hands, and let the mountaines reioyce together
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
9 Before the Lord: for he is come to iudge the earth: with righteousnesse shall hee iudge the world, and the people with equitie.
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.

< Psalms 98 >