< Psalms 9 >

1 To him that excelleth vpon Muth Laben. A Psalme of Dauid. I will praise the Lord with my whole heart: I will speake of all thy marueilous workes.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 I will bee glad, and reioyce in thee: I will sing praise to thy Name, O most High,
Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 For that mine enemies are turned backe: they shall fall, and perish at thy presence.
Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 For thou hast maintained my right and my cause: thou art set in the throne, and iudgest right.
Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 Thou hast rebuked the heathen: thou hast destroyed the wicked: thou hast put out their name for euer and euer.
Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 O enemie, destructions are come to a perpetual end, and thou hast destroyed the cities: their memoriall is perished with them.
Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 But the Lord shall sit for euer: hee hath prepared his throne for iudgement.
Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 For he shall iudge the worlde in righteousnes, and shall iudge the people with equitie.
Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 The Lord also wil be a refuge for the poore, a refuge in due time, euen in affliction.
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
10 And they that know thy Name, will trust in thee: for thou, Lord, hast not failed them that seeke thee.
Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Sing praises to the Lord, which dwelleth in Zion: shewe the people his workes.
Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 For whe he maketh inquisition for blood, hee remembreth it, and forgetteth not the complaint of the poore.
Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Haue mercie vpon mee, O Lord: consider my trouble which I suffer of them that hate mee, thou that liftest me vp from the gates of death,
Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 That I may shewe all thy praises within the gates of the daughter of Zion, and reioyce in thy saluation.
kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 The heathen are sunken downe in the pit that they made: in the nette that they hid, is their foote taken.
Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 The Lord is knowen by executing iudgement: the wicked is snared in the worke of his owne handes. (Higgaion, Selah)
Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
17 The wicked shall turne into hell, and all nations that forget God. (Sheol h7585)
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
18 For the poore shall not bee alway forgotten: the hope of the afflicted shall not perish for euer.
Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Vp Lord: let not man preuaile: let the heathen be iudged in thy sight.
Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Put them in feare, O Lord, that the heathen may knowe that they are but men. (Selah)
Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)

< Psalms 9 >